< Masalimo 50 >

1 Salimo la Asafu. Wamphamvuyo, Yehova Mulungu, akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
A Melody of Asaph. El, Elohim, Yahweh, hath spoken, and culled the earth, From the rising of the sun, unto the going in thereof:
2 Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri Mulungu akuwala.
Out of Zion the perfection of beauty, God, hath shone forth.
3 Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete; moto ukunyeketsa patsogolo pake, ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
Let our God come, and let him not keep silence! A fire—before him, shall devour, And, around him, hath it become exceeding tempestuous:
4 Iye akuyitanitsa zamumlengalenga ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
He calleth, Unto the heavens above, And unto the earth, That he may judge his people.
5 Mundisonkhanitsire okhulupirika anga, amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
Gather yourselves unto me—ye my men of lovingkindness, Who have solemnised my covenant over sacrifice.
6 Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake, pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
Now have the heavens declared his righteousness, Because, God, is, about to judge. (Selah)
7 Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula, iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa; ndine Mulungu, Mulungu wako.
Hear, O my people, and I will speak, O Israel, and I will adjure thee, God, thine own God, I am: —
8 Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako, kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
Not, for thy sacrifices, will I reprove thee, Nor for thine ascending-offerings, before me continually:
9 Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako kapena mbuzi za mʼkhola lako,
I will not take out of thy house—a bullock, Nor out of thy folds—he-goats;
10 pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
For, mine, is every wild-beast of the forest, The cattle on the mountains, in their thousands;
11 Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
I know every bird of the mountains, And, the moving things of the plain, are with me:
12 Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
If I were hungry, I would not tell thee, For, mine, is the world, and the fulness thereof.
13 Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna kapena kumwa magazi a mbuzi?
Will I eat the flesh of mighty oxen? Or, the blood of he-goats, will I drink?
14 “Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu, kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
Sacrifice to God a thankoffering, And pay to the Most High thy vows;
15 Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso; Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
Call upon me, then, in the day of distress, I will deliver thee, that thou mayest glorify me.
16 Koma kwa woyipa, Mulungu akuti, “Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
But, to the lawless one, God saith, What hast, thou, to do, to recount my statutes? Or that thou hast taken up my covenant upon thy mouth?
17 Iwe umadana ndi malangizo anga ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
Seeing that, thou, hast hated correction, And hast cast my words behind thee;
18 Ukaona wakuba umamutsatira, umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
If thou sawest a thief, then didst thou run with him, —And, with adulterers, hath been thy chosen life;
19 Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
Thy mouth, hast thou thrust into wickedness, And, thy tongue, kept weaving deceit;
20 Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
Thou wouldst sit down—Against thine own brother, wouldst thou speak, Against thine own mother’s son, wouldst thou expose a fault: —
21 Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete; umaganiza kuti ndine wofanana nawe koma ndidzakudzudzula ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
These things, hast thou done, and I have kept silence, Thou thoughtest that I should really be like thyself, I will convict thee, yea I will set [thine offences] in order before thine eyes.
22 “Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
Understand this, I pray you, ye forgetters of GOD, Lest I tear in pieces, and there be none to deliver: —
23 Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza, ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse chipulumutso cha Mulungu.”
He that sacrificeth a thankoffering, will glorify me, —And will prepare a way by which I may show him the salvation of God.

< Masalimo 50 >