< Masalimo 50 >

1 Salimo la Asafu. Wamphamvuyo, Yehova Mulungu, akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
A Psalm of Asaph. The God of gods, the Lord has spoken, and he has called the earth, from the rising of the sun even to its setting,
2 Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri Mulungu akuwala.
from Zion, the brilliance of his beauty.
3 Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete; moto ukunyeketsa patsogolo pake, ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
God will arrive manifestly. Our God also will not keep silence. A fire will flare up in his sight, and a mighty tempest will surround him.
4 Iye akuyitanitsa zamumlengalenga ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
He will call to heaven from above, and to the earth, to discern his people.
5 Mundisonkhanitsire okhulupirika anga, amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
Gather his holy ones to him, you who order his covenant above sacrifices.
6 Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake, pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
And the heavens will announce his justice. For God is the judge.
7 Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula, iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa; ndine Mulungu, Mulungu wako.
Listen, my people, and I will speak. Listen, Israel, and I will testify for you. I am God, your God.
8 Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako, kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
I will not reprove you for your sacrifices. Moreover, your holocausts are ever in my sight.
9 Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako kapena mbuzi za mʼkhola lako,
I will not accept calves from your house, nor he-goats from your flocks.
10 pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
For all the wild beasts of the forest are mine: the cattle on the hills and the oxen.
11 Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
I know all the flying things of the air, and the beauty of the field is with me.
12 Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
If I should be hungry, I would not tell you: for the whole world is mine, and all its plentitude.
13 Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna kapena kumwa magazi a mbuzi?
Shall I gnaw on the flesh of bulls? Or would I drink the blood of goats?
14 “Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu, kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
Offer to God the sacrifice of praise, and pay your vows to the Most High.
15 Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso; Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
And call upon me in the day of tribulation. I will rescue you, and you will honor me.
16 Koma kwa woyipa, Mulungu akuti, “Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
But to the sinner, God has said: Why do you discourse on my justices, and take up my covenant through your mouth?
17 Iwe umadana ndi malangizo anga ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
Truly, you have hated discipline, and you have cast my sermons behind you.
18 Ukaona wakuba umamutsatira, umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
If you saw a thief, you ran with him, and you have placed your portion with adulterers.
19 Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
Your mouth has abounded with malice, and your tongue has concocted deceits.
20 Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
Sitting, you spoke against your brother, and you set up a scandal against your mother’s son.
21 Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete; umaganiza kuti ndine wofanana nawe koma ndidzakudzudzula ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
These things you have done, and I was silent. You thought, unjustly, that I ought to be like you. But I will reprove you, and I will set myself against your face.
22 “Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
Understand these things, you who forget God; lest at any time, he might quickly take you away, and there would be no one to rescue you.
23 Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza, ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse chipulumutso cha Mulungu.”
The sacrifice of praise will honor me. And in that place is the journey by which I will reveal to him the salvation of God.

< Masalimo 50 >