< Masalimo 50 >

1 Salimo la Asafu. Wamphamvuyo, Yehova Mulungu, akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
En Psalme af Asaf. Den Almægtige, Gud Herren har talt og kaldet ad Jorden, fra Solens Opgang indtil dens Nedgang.
2 Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri Mulungu akuwala.
Fra Zion, Skønhedens Krone, aabenbarede Gud sig herligt.
3 Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete; moto ukunyeketsa patsogolo pake, ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
Vor Gud skal komme og ikke tie; en Ild for hans Ansigt skal fortære, og omkring ham stormer det saare.
4 Iye akuyitanitsa zamumlengalenga ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
Han kalder ad Himmelen oventil og ad Jorden for at dømme sit Folk.
5 Mundisonkhanitsire okhulupirika anga, amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
„Samler mig mine hellige, som have sluttet Pagt med mig ved Offer‟.
6 Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake, pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
Og Himlene kundgjorde hans Retfærdighed; thi Gud, han er Dommer. (Sela)
7 Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula, iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa; ndine Mulungu, Mulungu wako.
Hør, mit Folk, og jeg vil tale; Israel! og jeg vil vidne imod dig; jeg er Gud, din Gud.
8 Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako, kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
Jeg vil ikke gaa i Rette med dig for dine Slagtofre og for dine Brændofre, som ere altid for mig.
9 Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako kapena mbuzi za mʼkhola lako,
Jeg vil ikke tage en Okse af dit Hus, ej heller Bukke af dine Stalde.
10 pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
Thi alle Dyrene i Skoven høre mig til, Dyrene paa Bjergene i Tusindtal.
11 Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
Jeg kender alle Fuglene paa Bjergene, og hvad der vrimler paa Marken, er hos mig.
12 Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
Dersom jeg hungrede, vilde jeg ikke sige dig det; thi Jorderige hører mig til og dets Fylde.
13 Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna kapena kumwa magazi a mbuzi?
Skulde jeg vel æde Oksers Kød eller drikke Bukkes Blod?
14 “Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu, kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
Offer Gud Taksigelse og betal den Højeste dine Løfter!
15 Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso; Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
Og kald paa mig paa Nødens Dag; jeg vil udfri dig, og du skal ære mig.
16 Koma kwa woyipa, Mulungu akuti, “Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
Men til den ugudelige siger Gud: Hvad kommer det dig ved at tale om mine Skikke og at tage min Pagt i din Mund,
17 Iwe umadana ndi malangizo anga ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
da du dog hader Tugt og kaster mine Ord bag dig?
18 Ukaona wakuba umamutsatira, umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
Dersom du ser en Tyv, da er du Ven med ham, og med Horkarle er din Del.
19 Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
Du skikker din Mund til ondt, og med din Tunge digter du Svig.
20 Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
Du sidder og taler imod din Broder, du sætter Klik paa din Moders Søn.
21 Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete; umaganiza kuti ndine wofanana nawe koma ndidzakudzudzula ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
Disse Ting har du gjort, og jeg har tiet; du har tænkt, at jeg vel var som du; men jeg vil straffe dig og stille det frem for dine Øjne.
22 “Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
Forstaar dog dette, I, som have glemt Gud! at jeg ikke skal rive bort, og der ingen er, som frier.
23 Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza, ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse chipulumutso cha Mulungu.”
Den, som ofrer Taksigelse, han ærer mig, og den, som agter paa Vejen, ham vil jeg lade se Guds Frelse.

< Masalimo 50 >