< Masalimo 50 >
1 Salimo la Asafu. Wamphamvuyo, Yehova Mulungu, akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
Psalam. Asafov. Bog nad bogovima, Jahve, govori i zove zemlju od izlaza sunčeva do zalaza.
2 Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri Mulungu akuwala.
Sa Siona predivnog Bog zablista:
3 Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete; moto ukunyeketsa patsogolo pake, ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
Bog naš dolazi i ne šuti. Pred njim ide oganj što proždire, oko njega silna bjesni oluja.
4 Iye akuyitanitsa zamumlengalenga ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
On zove nebesa odozgo i zemlju da sudi narodu svojemu:
5 Mundisonkhanitsire okhulupirika anga, amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
“Saberite mi sve pobožnike koji žrtvom Savez sa mnom sklopiše!”
6 Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake, pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
Nebesa objavljuju pravednost njegovu: on je Bog sudac!
7 Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula, iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa; ndine Mulungu, Mulungu wako.
“Slušaj, narode moj, ja ću govoriti, o Izraele, svjedočit ću protiv tebe: ja, Bog - Bog tvoj!
8 Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako, kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
Ne korim te zbog žrtava tvojih - paljenice su tvoje svagda preda mnom.
9 Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako kapena mbuzi za mʼkhola lako,
Neću od doma tvog' uzet junca, ni jaraca iz tvojih torova:
10 pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
tÓa moje su sve životinje šumske, tisuće zvjeradi u gorama mojim.
11 Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
Znam sve ptice nebeske, moje je sve što se miče u poljima.
12 Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
Kad bih ogladnio, ne bih ti rekao, jer moja je zemlja i sve što je ispunja.
13 Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna kapena kumwa magazi a mbuzi?
Zar da ja jedem meso bikova ili da pijem krv jaraca?
14 “Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu, kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
Prinesi Bogu žrtvu zahvalnu, ispuni Višnjemu zavjete svoje!
15 Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso; Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
I zazovi me u dan tjeskobe: oslobodit ću te, a ti ćeš me slaviti.”
16 Koma kwa woyipa, Mulungu akuti, “Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
A grešniku Bog progovara: “Što tumačiš naredbe moje, što mećeš u usta Savez moj?
17 Iwe umadana ndi malangizo anga ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
Ti, komu stega ne prija, te riječi moje iza leđa bacaš?
18 Ukaona wakuba umamutsatira, umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
Kad tata vidiš, s njime se bratimiš i družiš se s preljubnicima.
19 Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
Svoja si usta predao pakosti, a jezik ti plete prijevare.
20 Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
U društvu na brata govoriš i kaljaš sina matere svoje.
21 Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete; umaganiza kuti ndine wofanana nawe koma ndidzakudzudzula ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
Sve si to činio, a ja da šutim? Zar misliš da sam ja tebi sličan? Pokarat ću te i stavit ću ti sve to pred oči.”
22 “Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
Shvatite ovo svi vi koji Boga zaboraviste, da vas ne pograbim i nitko vas spasiti neće.
23 Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza, ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse chipulumutso cha Mulungu.”
Pravo me štuje onaj koji prinosi žrtvu zahvalnu: i onomu koji hodi stazama pravim - njemu ću pokazati spasenje svoje.