< Masalimo 50 >
1 Salimo la Asafu. Wamphamvuyo, Yehova Mulungu, akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
亞薩的詩。 大能者上帝-耶和華已經發言招呼天下, 從日出之地到日落之處。
2 Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri Mulungu akuwala.
從全美的錫安中, 上帝已經發光了。
3 Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete; moto ukunyeketsa patsogolo pake, ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
我們的上帝要來,決不閉口。 有烈火在他面前吞滅; 有暴風在他四圍大颳。
4 Iye akuyitanitsa zamumlengalenga ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
他招呼上天下地, 為要審判他的民,
5 Mundisonkhanitsire okhulupirika anga, amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
說:招聚我的聖民到我這裏來, 就是那些用祭物與我立約的人。
6 Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake, pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
諸天必表明他的公義, 因為上帝是施行審判的。 (細拉)
7 Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula, iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa; ndine Mulungu, Mulungu wako.
我的民哪,你們當聽我的話! 以色列啊,我要勸戒你; 我是上帝,是你的上帝!
8 Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako, kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
我並不因你的祭物責備你; 你的燔祭常在我面前。
9 Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako kapena mbuzi za mʼkhola lako,
我不從你家中取公牛, 也不從你圈內取山羊;
10 pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
因為,樹林中的百獸是我的, 千山上的牲畜也是我的。
11 Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
山中的飛鳥,我都知道; 野地的走獸也都屬我。
12 Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
我若是飢餓,我不用告訴你, 因為世界和其中所充滿的都是我的。
13 Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna kapena kumwa magazi a mbuzi?
我豈吃公牛的肉呢? 我豈喝山羊的血呢?
14 “Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu, kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
你們要以感謝為祭獻與上帝, 又要向至高者還你的願,
15 Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso; Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
並要在患難之日求告我; 我必搭救你,你也要榮耀我。
16 Koma kwa woyipa, Mulungu akuti, “Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
但上帝對惡人說:你怎敢傳說我的律例, 口中提到我的約呢?
17 Iwe umadana ndi malangizo anga ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
其實你恨惡管教, 將我的言語丟在背後。
18 Ukaona wakuba umamutsatira, umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
你見了盜賊就樂意與他同夥, 又與行姦淫的人一同有分。
19 Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
你口任說惡言; 你舌編造詭詐。
20 Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
你坐着毀謗你的兄弟, 讒毀你親母的兒子。
21 Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete; umaganiza kuti ndine wofanana nawe koma ndidzakudzudzula ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
你行了這些事,我還閉口不言, 你想我恰和你一樣; 其實我要責備你,將這些事擺在你眼前。
22 “Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
你們忘記上帝的,要思想這事, 免得我把你們撕碎,無人搭救。
23 Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza, ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse chipulumutso cha Mulungu.”
凡以感謝獻上為祭的便是榮耀我; 那按正路而行的,我必使他得着我的救恩。