< Masalimo 5 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe zoyimbira za zitoliro. Salimo la Davide. Tcherani khutu ku mawu anga, Inu Yehova, ganizirani za kusisima kwanga
För sångmästaren, till Nehilót; en psalm av David. Lyssna till mina ord, HERRE; förnim min suckan.
2 Mverani kulira kwanga kofuna thandizo, Mfumu yanga ndi Mulungu wanga, pakuti kwa Inu, ine ndikupemphera.
Akta på mitt klagorop, du min konung och min Gud; ty till dig vill jag ställa min bön.
3 Mmawa, Yehova mumamva mawu anga; Mmawa ndimayala zopempha zanga pamaso panu ndi kudikira mwachiyembekezo.
HERRE, bittida hör du nu min röst, bittida frambär jag mitt offer till dig och skådar efter dig.
4 Inu si Mulungu amene mumasangalala ndi zoyipa; choyipa sichikhala pamaso panu.
Ty du är icke en Gud som har behag till ogudaktighet; den som är ond får icke bo hos dig.
5 Onyada sangathe kuyima pamaso panu; Inu mumadana ndi onse ochita zoyipa.
De övermodiga bestå icke inför dina ögon; du hatar alla ogärningsmän.
6 Mumawononga iwo amene amanena mabodza; anthu akupha ndi achinyengo, Yehova amanyansidwa nawo.
Du förgör dem som tala lögn; de blodgiriga och falska äro en styggelse för HERREN.
7 Koma Ine, mwa chifundo chanu chachikulu, ndidzalowa mʼNyumba yanu; mwa ulemu ndidzaweramira pansi kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera.
Men jag får gå in i ditt hus, genom din stora nåd; jag får tillbedja i din fruktan, vänd mot ditt heliga tempel.
8 Tsogolereni Inu Yehova, mwa chilungamo chanu chifukwa cha adani anga ndipo wongolani njira yanu pamaso panga.
HERRE, led mig genom din rättfärdighet, för mina förföljares skull; gör din väg jämn för mig.
9 Palibe mawu ochokera mʼkamwa mwawo amene angadalirike; mtima wawo wadzaza ndi chiwonongeko. Kummero kwawo kuli ngati manda apululu; ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.
Ty i deras mun är intet visst, deras innersta är fördärv, en öppen grav är deras strupe, sin tunga göra de hal.
10 Lengezani kuti ndi olakwa, Inu Mulungu! Zochita zawo zoyipa zikhale kugwa kwawo. Achotseni pamaso panu chifukwa cha machimo awo ambiri, pakuti awukira Inu.
Döm dem, o Gud; må de komma på fall med sina anslag. Driv bort dem för deras många överträdelsers skull, eftersom de äro gensträviga mot dig.
11 Koma lolani kuti onse amene apeza chitetezo mwa Inu akondwere; lolani kuti aziyimba nthawi zonse chifukwa cha chimwemwe. Aphimbeni ndi chitetezo chanu, iwo amene amakonda dzina lanu akondwere mwa Inu.
Men låt alla dem glädjas, som taga sin tillflykt till dig; evinnerligen må de jubla, ty du beskärmar dem; i dig må de fröjda sig, som hava ditt namn kärt.
12 Ndithu, Inu Yehova, mumadalitsa olungama; mumawazungulira ndi kukoma mtima kwanu ngati chishango.
Ty du, HERRE, välsignar den rättfärdige; du betäcker honom med nåd såsom med en sköld.

< Masalimo 5 >