< Masalimo 5 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe zoyimbira za zitoliro. Salimo la Davide. Tcherani khutu ku mawu anga, Inu Yehova, ganizirani za kusisima kwanga
برای رهبر سرایندگان: مزمور داوود، با همراهی سازهای بادی. ای خداوند، به سخنان من گوش بده و به نالهٔ من توجه فرما.
2 Mverani kulira kwanga kofuna thandizo, Mfumu yanga ndi Mulungu wanga, pakuti kwa Inu, ine ndikupemphera.
ای پادشاه و ای خدای من، به فریادم برس، زیرا من فقط نزد تو دعا می‌کنم.
3 Mmawa, Yehova mumamva mawu anga; Mmawa ndimayala zopempha zanga pamaso panu ndi kudikira mwachiyembekezo.
ای خداوند، صبحگاهان به پیشگاه تو دعا می‌کنم و تو صدای مرا می‌شنوی، پس من انتظار خواهم کشید تا جواب مرا بدهی.
4 Inu si Mulungu amene mumasangalala ndi zoyipa; choyipa sichikhala pamaso panu.
تو خدایی نیستی که گناه را دوست بداری و شرارت را تحمل کنی.
5 Onyada sangathe kuyima pamaso panu; Inu mumadana ndi onse ochita zoyipa.
تو تحمل دیدن متکبران را نداری و از همهٔ بدکاران نفرت داری.
6 Mumawononga iwo amene amanena mabodza; anthu akupha ndi achinyengo, Yehova amanyansidwa nawo.
ای خداوند، تو از قاتلان و حیله‌گران بیزاری و دروغگویان را هلاک می‌کنی.
7 Koma Ine, mwa chifundo chanu chachikulu, ndidzalowa mʼNyumba yanu; mwa ulemu ndidzaweramira pansi kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera.
اما من در پناه محبت عظیم تو به خانهٔ مقدّست داخل خواهم شد و با ترس و احترام، تو را عبادت خواهم کرد.
8 Tsogolereni Inu Yehova, mwa chilungamo chanu chifukwa cha adani anga ndipo wongolani njira yanu pamaso panga.
ای خداوند عادل، راه خود را به من نشان ده و مرا هدایت نما تا دشمنانم نتوانند بر من چیره شوند.
9 Palibe mawu ochokera mʼkamwa mwawo amene angadalirike; mtima wawo wadzaza ndi chiwonongeko. Kummero kwawo kuli ngati manda apululu; ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.
به سخنان دهانشان نمی‌توان اعتماد کرد و دلشان مملو از شرارت است. گلویشان گوری است گشاده، و دروغ بر زبانشان است.
10 Lengezani kuti ndi olakwa, Inu Mulungu! Zochita zawo zoyipa zikhale kugwa kwawo. Achotseni pamaso panu chifukwa cha machimo awo ambiri, pakuti awukira Inu.
ای خدا، تو آنها را محکوم کن و بگذار خود در دامهایشان گرفتار شوند! آنها را دور بینداز، زیرا گناهان زیادی مرتکب شده‌اند و بر ضد تو برخاسته‌اند.
11 Koma lolani kuti onse amene apeza chitetezo mwa Inu akondwere; lolani kuti aziyimba nthawi zonse chifukwa cha chimwemwe. Aphimbeni ndi chitetezo chanu, iwo amene amakonda dzina lanu akondwere mwa Inu.
اما بگذار همهٔ کسانی که به تو پناه می‌آورند، خوشحال شوند و همیشه با شادی سرود بخوانند. از کسانی که تو را دوست دارند محافظت نما تا آنها در پناه تو شادمان باشند.
12 Ndithu, Inu Yehova, mumadalitsa olungama; mumawazungulira ndi kukoma mtima kwanu ngati chishango.
تو ای خداوند، عادلان را برکت می‌دهی و ایشان را با سپر محبت خود محافظت می‌نمایی.

< Masalimo 5 >