< Masalimo 5 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe zoyimbira za zitoliro. Salimo la Davide. Tcherani khutu ku mawu anga, Inu Yehova, ganizirani za kusisima kwanga
Dāvida dziesma. Dziedātāju vadonim uz stabulēm. Ak Kungs, klausies uz maniem vārdiem, ņem vērā manas domas.
2 Mverani kulira kwanga kofuna thandizo, Mfumu yanga ndi Mulungu wanga, pakuti kwa Inu, ine ndikupemphera.
Samani manas kliegšanas balsi, mans ķēniņ un mans Dievs, jo es Tevi gribu pielūgt.
3 Mmawa, Yehova mumamva mawu anga; Mmawa ndimayala zopempha zanga pamaso panu ndi kudikira mwachiyembekezo.
Rītos, ak Kungs, klausi manu balsi, rītos es uz Tevi gribu sataisīties un skatīties.
4 Inu si Mulungu amene mumasangalala ndi zoyipa; choyipa sichikhala pamaso panu.
Jo Tu neesi tāds Dievs, kam bezdievība patīk; kas ir ļauns, tas pie Tevis nepaliek.
5 Onyada sangathe kuyima pamaso panu; Inu mumadana ndi onse ochita zoyipa.
Trakotāji nepastāvēs priekš Tavām acīm, Tu ienīsti visus ļauna darītājus.
6 Mumawononga iwo amene amanena mabodza; anthu akupha ndi achinyengo, Yehova amanyansidwa nawo.
Tu nomaitā melkuļus, asins vainīgie un viltnieki Tam Kungam ir negantība.
7 Koma Ine, mwa chifundo chanu chachikulu, ndidzalowa mʼNyumba yanu; mwa ulemu ndidzaweramira pansi kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera.
Bet es iešu Tavā namā caur Tavu lielo žēlastību, es pielūgšu Tava svētuma mājoklī, Tevi bīdamies.
8 Tsogolereni Inu Yehova, mwa chilungamo chanu chifukwa cha adani anga ndipo wongolani njira yanu pamaso panga.
Kungs, vadi mani pēc Savas taisnības, manu glūnētāju dēļ, dari līdzenu Savu ceļu manā priekšā.
9 Palibe mawu ochokera mʼkamwa mwawo amene angadalirike; mtima wawo wadzaza ndi chiwonongeko. Kummero kwawo kuli ngati manda apululu; ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.
Jo viņu mutē nav nekādas patiesības, viņu sirdīs ir ļaunums, viņu rīkle ir atvērts kaps, ar savu mēli tie glauda.
10 Lengezani kuti ndi olakwa, Inu Mulungu! Zochita zawo zoyipa zikhale kugwa kwawo. Achotseni pamaso panu chifukwa cha machimo awo ambiri, pakuti awukira Inu.
Sodi tos, ak Dievs, lai tie krīt no saviem padomiem; atstum tos viņu lielos noziegumos, jo tie pret Tevi sacēlušies,
11 Koma lolani kuti onse amene apeza chitetezo mwa Inu akondwere; lolani kuti aziyimba nthawi zonse chifukwa cha chimwemwe. Aphimbeni ndi chitetezo chanu, iwo amene amakonda dzina lanu akondwere mwa Inu.
Bet lai priecājās visi, kas uz Tevi cerē, mūžīgi lai tie gavilē, jo Tu tos pasargi; lai līksmojās iekš Tevis, kas Tavu vārdu mīļo.
12 Ndithu, Inu Yehova, mumadalitsa olungama; mumawazungulira ndi kukoma mtima kwanu ngati chishango.
Jo Tu, Kungs, svētīsi to taisno, un to pušķosi ar žēlastību kā ar bruņām.