< Masalimo 5 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe zoyimbira za zitoliro. Salimo la Davide. Tcherani khutu ku mawu anga, Inu Yehova, ganizirani za kusisima kwanga
Denggem ti awagko kenka, O Yahweh; panunotem dagiti as-asugko.
2 Mverani kulira kwanga kofuna thandizo, Mfumu yanga ndi Mulungu wanga, pakuti kwa Inu, ine ndikupemphera.
Denggem ti timek ti awagko, O Arik ken Diosko, ta sika ti pagkarkararagak.
3 Mmawa, Yehova mumamva mawu anga; Mmawa ndimayala zopempha zanga pamaso panu ndi kudikira mwachiyembekezo.
O Yahweh, mangmangngegmo ti ararawko iti agsapa; iti agsapa, iyegko dagiti kiddawko kenka ken agurayak a sinanama.
4 Inu si Mulungu amene mumasangalala ndi zoyipa; choyipa sichikhala pamaso panu.
Pudno a saanka a Dios nga uman-anamong iti dakes; saanto a dagiti dakes a tattao ti sangailim.
5 Onyada sangathe kuyima pamaso panu; Inu mumadana ndi onse ochita zoyipa.
Saanto nga agtakder iti imatangmo dagiti napalangguad a tattao; kagurguram dagiti amin nga agtitignay a sidadangkes.
6 Mumawononga iwo amene amanena mabodza; anthu akupha ndi achinyengo, Yehova amanyansidwa nawo.
Dadaelemto dagiti ulbod; um-umsien ni Yahweh dagiti naranggas ken manangallilaw a tattao.
7 Koma Ine, mwa chifundo chanu chachikulu, ndidzalowa mʼNyumba yanu; mwa ulemu ndidzaweramira pansi kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera.
Ngem para kaniak, gapu iti naindaklan a kinapudnom iti tulagmo, sumrekak iti balaymo; siraraem nga agrukbabak iti nasantoan a templom.
8 Tsogolereni Inu Yehova, mwa chilungamo chanu chifukwa cha adani anga ndipo wongolani njira yanu pamaso panga.
O Apo, idalannak iti kinalintegmo gapu kadagiti kabusorko; palintegem ti dalanmo iti sangoanak.
9 Palibe mawu ochokera mʼkamwa mwawo amene angadalirike; mtima wawo wadzaza ndi chiwonongeko. Kummero kwawo kuli ngati manda apululu; ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.
Ta awan ti kinapudno iti ngiwatda; nadangkes ti kaungganda; ti karabukobda ket nakalukat a tanem; agpaspasablogda babaen iti dilada.
10 Lengezani kuti ndi olakwa, Inu Mulungu! Zochita zawo zoyipa zikhale kugwa kwawo. Achotseni pamaso panu chifukwa cha machimo awo ambiri, pakuti awukira Inu.
Ibilangmo a nagbiddutda, O Dios; dagiti panggepda koma ti pakatinnaganda! Papanawem ida gapu kadagiti adu a basbasolda, gapu ta nagsukirda kenka.
11 Koma lolani kuti onse amene apeza chitetezo mwa Inu akondwere; lolani kuti aziyimba nthawi zonse chifukwa cha chimwemwe. Aphimbeni ndi chitetezo chanu, iwo amene amakonda dzina lanu akondwere mwa Inu.
Ngem agrag-o koma dagiti amin nga agkamang kenka; ipalubosmo koma a kanayon nga agpukkawda a sirarag-o agsipud ta ikankanawam ida; ipalubosmo koma nga agrag-oda kenka, dagidiay mangay-ayat iti naganmo.
12 Ndithu, Inu Yehova, mumadalitsa olungama; mumawazungulira ndi kukoma mtima kwanu ngati chishango.
Ta bendisionamto dagiti nalinteg, O Yahweh; palikmutamto ida iti ayatmo a kas iti maysa a kalasag.