< Masalimo 5 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe zoyimbira za zitoliro. Salimo la Davide. Tcherani khutu ku mawu anga, Inu Yehova, ganizirani za kusisima kwanga
to/for to conduct to(wards) [the] flute melody to/for David word my to listen [emph?] LORD to understand [emph?] meditation my
2 Mverani kulira kwanga kofuna thandizo, Mfumu yanga ndi Mulungu wanga, pakuti kwa Inu, ine ndikupemphera.
to listen [emph?] to/for voice: sound to cry my king my and God my for to(wards) you to pray
3 Mmawa, Yehova mumamva mawu anga; Mmawa ndimayala zopempha zanga pamaso panu ndi kudikira mwachiyembekezo.
LORD morning to hear: hear voice my morning to arrange to/for you and to watch
4 Inu si Mulungu amene mumasangalala ndi zoyipa; choyipa sichikhala pamaso panu.
for not God delighting wickedness you(m. s.) not to sojourn you bad: evil
5 Onyada sangathe kuyima pamaso panu; Inu mumadana ndi onse ochita zoyipa.
not to stand to be foolish to/for before eye your to hate all to work evil: wickedness
6 Mumawononga iwo amene amanena mabodza; anthu akupha ndi achinyengo, Yehova amanyansidwa nawo.
to perish to speak: speak lie man: anyone blood and deceit to abhor LORD
7 Koma Ine, mwa chifundo chanu chachikulu, ndidzalowa mʼNyumba yanu; mwa ulemu ndidzaweramira pansi kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera.
and I in/on/with abundance kindness your to come (in): come house: home your to bow to(wards) temple holiness your in/on/with fear your
8 Tsogolereni Inu Yehova, mwa chilungamo chanu chifukwa cha adani anga ndipo wongolani njira yanu pamaso panga.
LORD to lead me in/on/with righteousness your because enemy my (to smooth *Q(k)*) to/for face: before my way: conduct your
9 Palibe mawu ochokera mʼkamwa mwawo amene angadalirike; mtima wawo wadzaza ndi chiwonongeko. Kummero kwawo kuli ngati manda apululu; ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.
for nothing in/on/with lip his to establish: right entrails: inner parts their desire grave to open throat their tongue their to smooth [emph?]
10 Lengezani kuti ndi olakwa, Inu Mulungu! Zochita zawo zoyipa zikhale kugwa kwawo. Achotseni pamaso panu chifukwa cha machimo awo ambiri, pakuti awukira Inu.
be guilty them God to fall: fall from counsel their in/on/with abundance transgression their to banish them for to rebel in/on/with you
11 Koma lolani kuti onse amene apeza chitetezo mwa Inu akondwere; lolani kuti aziyimba nthawi zonse chifukwa cha chimwemwe. Aphimbeni ndi chitetezo chanu, iwo amene amakonda dzina lanu akondwere mwa Inu.
and to rejoice all to seek refuge in/on/with you to/for forever: enduring to sing and to cover upon them and to rejoice in/on/with you to love: lover name your
12 Ndithu, Inu Yehova, mumadalitsa olungama; mumawazungulira ndi kukoma mtima kwanu ngati chishango.
for you(m. s.) to bless righteous LORD like/as shield acceptance to surround him

< Masalimo 5 >