< Masalimo 5 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe zoyimbira za zitoliro. Salimo la Davide. Tcherani khutu ku mawu anga, Inu Yehova, ganizirani za kusisima kwanga
Unto the end. For her who pursues the inheritance. A Psalm of David. O Lord, listen closely to my words. Understand my outcry.
2 Mverani kulira kwanga kofuna thandizo, Mfumu yanga ndi Mulungu wanga, pakuti kwa Inu, ine ndikupemphera.
Attend to the voice of my prayer, my King and my God.
3 Mmawa, Yehova mumamva mawu anga; Mmawa ndimayala zopempha zanga pamaso panu ndi kudikira mwachiyembekezo.
For to you, I will pray. In the morning, Lord, you will hear my voice.
4 Inu si Mulungu amene mumasangalala ndi zoyipa; choyipa sichikhala pamaso panu.
In the morning, I will stand before you, and I will see. For you are not a God who wills iniquity.
5 Onyada sangathe kuyima pamaso panu; Inu mumadana ndi onse ochita zoyipa.
And the malicious will not dwell close to you, nor will the unjust endure before your eyes.
6 Mumawononga iwo amene amanena mabodza; anthu akupha ndi achinyengo, Yehova amanyansidwa nawo.
You hate all who work iniquity. You will destroy all who speak a lie. The bloody and deceitful man, the Lord will abominate.
7 Koma Ine, mwa chifundo chanu chachikulu, ndidzalowa mʼNyumba yanu; mwa ulemu ndidzaweramira pansi kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera.
But I am in the multitude of your mercy. I will enter your house. I will show adoration toward your holy temple, in your fear.
8 Tsogolereni Inu Yehova, mwa chilungamo chanu chifukwa cha adani anga ndipo wongolani njira yanu pamaso panga.
Lord, lead me in your justice. Because of my enemies, direct my way in your sight.
9 Palibe mawu ochokera mʼkamwa mwawo amene angadalirike; mtima wawo wadzaza ndi chiwonongeko. Kummero kwawo kuli ngati manda apululu; ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.
For there is no truth in their mouth: their heart is vain.
10 Lengezani kuti ndi olakwa, Inu Mulungu! Zochita zawo zoyipa zikhale kugwa kwawo. Achotseni pamaso panu chifukwa cha machimo awo ambiri, pakuti awukira Inu.
Their throat is an open sepulcher. They have acted deceitfully with their tongues. Judge them, O God. Let them fall by their own intentions: according to the multitude of their impiety, expel them. For they have provoked you, O Lord.
11 Koma lolani kuti onse amene apeza chitetezo mwa Inu akondwere; lolani kuti aziyimba nthawi zonse chifukwa cha chimwemwe. Aphimbeni ndi chitetezo chanu, iwo amene amakonda dzina lanu akondwere mwa Inu.
But let all those who hope in you rejoice. They will exult in eternity, and you will dwell in them. And all those who love your name will glory in you.
12 Ndithu, Inu Yehova, mumadalitsa olungama; mumawazungulira ndi kukoma mtima kwanu ngati chishango.
For you will bless the just. You have crowned us, O Lord, as if with a shield of your good will.

< Masalimo 5 >