< Masalimo 5 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe zoyimbira za zitoliro. Salimo la Davide. Tcherani khutu ku mawu anga, Inu Yehova, ganizirani za kusisima kwanga
JUNGOG, O Jeova, y sinanganjo, ecungog y jinasoco.
2 Mverani kulira kwanga kofuna thandizo, Mfumu yanga ndi Mulungu wanga, pakuti kwa Inu, ine ndikupemphera.
Ecungog y vos y inagangjo, Ray jo, yan Yuusso: sa jago jutaetaetaye.
3 Mmawa, Yehova mumamva mawu anga; Mmawa ndimayala zopempha zanga pamaso panu ndi kudikira mwachiyembekezo.
O Jeova, y egaan unjungog y vosso; y egaan juguaguato y tinaetaejo guiya jago, ya jubébela.
4 Inu si Mulungu amene mumasangalala ndi zoyipa; choyipa sichikhala pamaso panu.
Sa ti jago na Yuus ni y gumaeya y tinaelaye: y taelaye ti usaga guiya jago.
5 Onyada sangathe kuyima pamaso panu; Inu mumadana ndi onse ochita zoyipa.
Ti manasaga y mangaduco gui menan matamo: ya ti yamo todo y fumatitinas y taelaye.
6 Mumawononga iwo amene amanena mabodza; anthu akupha ndi achinyengo, Yehova amanyansidwa nawo.
Jago yumulang y manguecuentos mandague: ya y taotao cajâgâ yan y dinague, si Jeova jaguefchatlie.
7 Koma Ine, mwa chifundo chanu chachikulu, ndidzalowa mʼNyumba yanu; mwa ulemu ndidzaweramira pansi kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera.
Ya guajoja, yan y megagae y minaasemo, bae jalom gui guimamo: ya juadora anae juatan y santo templomo ni y ninamaañaomo.
8 Tsogolereni Inu Yehova, mwa chilungamo chanu chifukwa cha adani anga ndipo wongolani njira yanu pamaso panga.
O Jeova, esgaejonyo gui tininasmo, pot causa ya enimigujo; natunas gui menajo y chalanmo.
9 Palibe mawu ochokera mʼkamwa mwawo amene angadalirike; mtima wawo wadzaza ndi chiwonongeko. Kummero kwawo kuli ngati manda apululu; ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.
Sa taya finitme gui pachotñija; ya sanjalomñija senmanaelaye: naftan mababa y agagañija; yan y jilañija finande:
10 Lengezani kuti ndi olakwa, Inu Mulungu! Zochita zawo zoyipa zikhale kugwa kwawo. Achotseni pamaso panu chifukwa cha machimo awo ambiri, pakuti awukira Inu.
Condena sija, O Yuus, polo y ufamodong pot y pinagatñija: gui minegae y isaoñija nasuja sija sa managuaguat contra jago.
11 Koma lolani kuti onse amene apeza chitetezo mwa Inu akondwere; lolani kuti aziyimba nthawi zonse chifukwa cha chimwemwe. Aphimbeni ndi chitetezo chanu, iwo amene amakonda dzina lanu akondwere mwa Inu.
Nafanmagof todos y umangngocojao, polo para taejinecog ya ufanagang pot y minagofñija sa undefiende sija, polo ya ufanmagof ni jago, y gumaeya y naanmo.
12 Ndithu, Inu Yehova, mumadalitsa olungama; mumawazungulira ndi kukoma mtima kwanu ngati chishango.
Sa jago bumendise y manunas; O Jeova, parejoja yan un patang unpolo gui oriyaña y finaborese.

< Masalimo 5 >