< Masalimo 49 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
Керівнику хору. Синів Кореєвих псалом. Послухайте це, усі народи, зважте, усі мешканці плинного світу,
2 anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
сини Адамові, сини людські, – як багаті, так і бідні.
3 Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
Вуста мої промовлять мудрість, і роздуми мого серця – [глибоке] розуміння.
4 Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
Схилю своє вухо до притчі, відкрию під [звуки] арфи мою загадку:
5 Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
Чого мені боятися в дні лиха, коли беззаконня лукавих оточить мене –
6 Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
тих, хто на власні статки покладає надію й багатством своїм вихваляється?
7 Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
Але ж брата ніхто не зможе викупити, ніхто не дасть Богові [належного] викупу за нього.
8 Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
Бо занадто дорогим [був би] викуп за його душу, тому повік не досягти того,
9 kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
щоб хтось жив вічно й не побачив безодні смерті.
10 Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
Адже кожен бачить, що мудрі помирають, і поряд із ними дурень і невіглас гине, залишаючи іншим свої статки.
11 Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
Могили стали для них вічним домом, помешканнями їхніми з роду в рід. А вони називали своїми іменами землі!
12 Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
Але ж людина не [завжди] перебуватиме в пошані, подібна вона до тварин, що гинуть.
13 Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
Так, [життєві] дороги їхні – невігластво! Однак їхні наступники схвалюють те, що в них на вустах.
14 Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol h7585)
Немов вівці, вони приготовані для царства смерті; смерть пастиме їх, а на ранок праведники пануватимуть над ними. Їхня міць виснажиться, безодня смерті – омріяне житло для них. (Sheol h7585)
15 Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol h7585)
Але Бог викупить душу мою з-під [влади] царства мертвих, коли прийме мене [до Себе]. (Села) (Sheol h7585)
16 Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
Не переймайся, коли хтось багатіє, коли посилюється слава дому його.
17 Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
Адже в час смерті нічого не візьме він із собою, слава його не зійде вслід за ним [до царства мертвих].
18 Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
Навіть якщо за життя він вважав себе благословенним, – адже хвалять тебе люди, коли ти добре собі робиш, –
19 iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
однак піде він до роду своїх предків, так що повік світла не побачить.
20 Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.
Людина в пошані, але нерозумна, подібна до тварин, що гинуть.

< Masalimo 49 >