< Masalimo 49 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
Oíd esto todos los pueblos: escuchád todos los habitadores del mundo:
2 anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
Así los hijos de los hombres como los hijos de los varones: juntamente el rico y el pobre.
3 Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
Mi boca hablará sabidurías: y el pensamiento de mi corazón inteligencias.
4 Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
Acomodaré a ejemplos mi oído: declararé con la arpa mi enigma.
5 Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
¿Por qué temeré en los días de adversidad, cuando la iniquidad de mis calcañares me cercará?
6 Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
Los que confían en sus haciendas, y en la multitud de sus riquezas se jactan;
7 Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
Ninguno redimiendo redimirá al hermano: ni dará a Dios su rescate.
8 Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
Porque la redención de su alma es de gran precio: y no se hará jamás,
9 kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
Que viva adelante para siempre: y nunca vea la sepultura.
10 Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
Porque se ve que los sabios mueren juntamente: el insensato y el ignorante perecen, y dejan a otros sus riquezas.
11 Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
En su íntimo piensan que sus casas son eternas: sus habitaciones para generación y generación: llamaron sus tierras de sus nombres.
12 Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
Mas el hombre no permanecerá en honra: es semejante a las bestias que mueren.
13 Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
Este es su camino, su locura: y sus descendientes corren por el dicho de ellos. (Selah)
14 Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol )
Como ovejas son puestos en la sepultura, la muerte los pastorea; y los rectos se enseñorearon de ellos por la mañana: y su apariencia se envejece en la sepultura de su morada. (Sheol )
15 Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol )
Ciertamente Dios redimirá mi vida del poder de la sepultura, cuando me tomará. (Selah) (Sheol )
16 Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
No temas cuando se enriquece alguno: cuando aumenta la gloria de su casa.
17 Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
Porque en su muerte no tomará nada: ni su gloria descenderá en pos de él.
18 Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
Porque mientras viviere, será su vida bendita: y tú serás loado cuando fueres bueno.
19 iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
El entrará a la generación de sus padres: para siempre no verán luz.
20 Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.
El hombre en honra que no entiende, semejante es a las bestias que mueren.