< Masalimo 49 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
Poslušajte to, vsa ve ljudstva, pazljivo prisluhnite, vsi vi prebivalci sveta,
2 anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
tako nizki kakor visoki, bogati in revni skupaj.
3 Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
Moja usta bodo govorila o modrosti in premišljevanje mojega srca bo o spoznanju.
4 Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
Svoje uho bom nagnil k prispodobi. Svoje mračne izjave bom razkrival na harfi.
5 Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
Zakaj naj bi se bal v dneh zla, ko me bo obdala krivičnost mojih petá?
6 Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
Tisti, ki zaupajo v svoje premoženje in se bahajo z množino svojih bogastev,
7 Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
nihče izmed njih ne more odkupiti svojega brata na kakršenkoli način niti Bogu dati odkupnine zanj
8 Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
(kajti odkupitev njihove duše je dragocena in primanjkuje na veke),
9 kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
da naj bi mirno živel na veke in ne videl trohnobe.
10 Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
Kajti vidi, da modri možje umrejo, prav tako se pogubita bedak in brutalna oseba in svoje premoženje zapustita drugim.
11 Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
Njihova notranja misel je, da bodo svoje hiše ohranili na veke in svoja bivališča za vse rodove; svoja zemljišča imenujejo po svojih imenih.
12 Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
Kljub temu človek, ki je v časti, ne ostane; podoben je živalim, ki poginejo.
13 Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
Ta njihova pot je njihova neumnost, vendar njihovo potomstvo odobrava njihove izjave. (Sela)
14 Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol h7585)
Kakor ovce so položeni v grob; z njimi se bo hranila smrt in iskreni bodo zjutraj imeli nad njimi oblast in njihova lepota bo požrta v grobu, proč od njihovega bivanja. (Sheol h7585)
15 Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol h7585)
Toda Bog bo mojo dušo odkupil iz oblasti groba, kajti sprejel me bo. (Sela) (Sheol h7585)
16 Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
Ne boj se, kadar nekdo bogatí, ko se slava njegove hiše množí,
17 Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
kajti ko umre, ne bo ničesar odnesel. Njegova slava se ne bo spustila za njim.
18 Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
Čeprav je, medtem ko je živel, blagoslavljal svojo dušo – ljudje te bodo hvalili, ko delaš dobro sebi.
19 iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
Šel bo k rodu svojih očetov; oni nikoli ne bodo videli svetlobe.
20 Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.
Človek, ki je v časti, pa ne spoznava, je podoben živalim, ki poginejo.

< Masalimo 49 >