< Masalimo 49 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
Przewodnikowi chóru. Psalm dla synów Korego. Słuchajcie tego wszystkie narody, nadstawcie ucha wszyscy mieszkańcy świata.
2 anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
Zarówno wy, prości, jak i wy, możni; zarówno bogaty, jak i ubogi.
3 Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
Moje usta wypowiedzą mądrość, a rozmyślaniem mego serca [będzie] roztropność.
4 Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
Nakłonię ucha ku przypowieści, przy harfie rozwiążę moją zagadkę.
5 Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
Dlaczego mam się bać w dniach niedoli, [gdy] otacza mnie nieprawość tych, którzy mnie depczą?
6 Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
Ci, którzy ufają swym bogactwom i chlubią się swym wielkim dostatkiem;
7 Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
Nikt [z nich] w żaden sposób nie odkupi swego brata ani nie może dać Bogu [za niego] okupu;
8 Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
(Kosztowny bowiem jest okup za ich dusze i nigdy się nie zdarzy);
9 kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
Aby żył na wieki i nie doznał zniszczenia.
10 Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
Każdy bowiem widzi, że mądrzy umierają, tak samo jak ginie głupiec i prostak, i zostawiają obcym swoje bogactwa.
11 Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
Myślą, [że] ich domy [są] wieczne, a ich mieszkania [będą trwać] z pokolenia na pokolenie; nazywają ziemie swymi imionami.
12 Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
Lecz człowiek, choć otoczony czcią, nie przetrwa; podobny jest do bydląt, które giną.
13 Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
Ich droga jest ich głupstwem, mimo to ich potomkowie pochwalają ich mowę. (Sela)
14 Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol )
Jak owce będą złożeni w grobie, śmierć ich pożre; prawi będą nad nimi panować o poranku, ich postać zostanie zniszczona w grobie, gdy opuszczą swoje mieszkanie. (Sheol )
15 Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol )
Ale Bóg wykupi moją duszę z mocy grobu, bo mnie przyjmie. (Sela) (Sheol )
16 Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
Nie bój się, gdy się ktoś wzbogaci, gdy się rozmnoży sława jego domu;
17 Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
Bo gdy umrze, niczego [ze sobą] nie weźmie i nie pójdzie za nim jego sława.
18 Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
Chociaż za życia swej duszy pochlebiał i chwalono go, gdy dobrze się urządził;
19 iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
Pójdzie jednak do grona swych ojców; nigdy nie ujrzą światła.
20 Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.
Człowiek, który jest otoczony czcią, a nie rozumie [tego], podobny jest do bydląt, które giną.