< Masalimo 49 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
Zwanini lokhu lonke bantu. Bekani indlebe lonke bakhileyo bomhlaba,
2 anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
bonke abantukazana labaphakemeyo, abanothileyo labayanga, ndawonye.
3 Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
Umlomo wami uzakhuluma izinhlakanipho, lokuzindla kwenhliziyo yami kuzakuba yikuqedisisa.
4 Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
Ngizabeka indlebe yami kuso isaga, ngizavula ilibho lami ngechacho.
5 Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
Ngizakwesabelani ensukwini zobubi, nxa ububi babagwenxi bami buzangihanqa.
6 Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
Abathemba ingcebo yabo, abazincoma ngobunengi benotho yabo,
7 Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
umuntu kasoze ahlenge lokuhlenga umfowabo, kasoze amnike uNkulunkulu inhlawulo yakhe,
8 Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
(ngoba uhlengo lomphefumulo wabo luligugu, futhi luyaphela laphakade)
9 kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
ukuze ahlale ephila phakade, angaboni ukubola.
10 Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
Ngoba ubona ukuthi abahlakaniphileyo bayafa, lokuthi isithutha kanye lesiphukuphuku bayabhubha, batshiyele inotho yabo abanye.
11 Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
Umcabango wabo wangaphakathi uyikuthi izindlu zabo zizakuba ngezaphakade, izindawo zabo zokuhlala zibe ngezezizukulwana, babize amazwe ngamabizo abo.
12 Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
Kodwa umuntu elodumo kayikuma, uyafanana lenyamazana ezibhubhayo.
13 Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
Le indlela yabo iyibuthutha babo; kube kanti ababalandelayo bathokoza ngomlomo wabo. (Sela)
14 Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol h7585)
Njengezimvu bamiselwe ingcwaba, ukufa kuzabelusa; labaqotho bazababusa ekuseni, isimo sabo ngesokuqedwa lingcwaba ukuze bangabi lendawo yokuhlala. (Sheol h7585)
15 Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol h7585)
Kodwa uNkulunkulu uzahlenga umphefumulo wami emandleni engcwaba, ngoba uzangemukela. (Sela) (Sheol h7585)
16 Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
Ungesabi nxa umuntu enotha, nxa udumo lwendlu yakhe lusanda;
17 Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
ngoba ekufeni kwakhe kayikuthatha lutho, udumo lwakhe kaluyikwehla lumlandele.
18 Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
Lanxa empilweni yakhe wabusisa umphefumulo wakhe, njalo bakudumisa nxa uzenzela okuhle,
19 iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
uzakuya esizukulwaneni saboyise, kabayikubona ukukhanya kuze kube phakade.
20 Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.
Umuntu olodumo, engaqedisisi, unjengezinyamazana ezibhubhayo.

< Masalimo 49 >