< Masalimo 49 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
Mazmur kaum Korah. Untuk pemimpin kor. Dengarlah, hai segala bangsa, pasanglah telinga, hai penduduk dunia,
2 anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
baik orang sederhana, maupun orang terkemuka, baik orang miskin, maupun orang kaya.
3 Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
Aku akan mengucapkan kata-kata bijaksana, buah pikiranku sangat dalam.
4 Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
Aku akan memperhatikan peribahasa, dan menerangkan artinya sambil memetik kecapi.
5 Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
Aku tidak takut di waktu kesesakan, waktu aku dikepung oleh musuh yang jahat.
6 Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
Mereka itu mengandalkan kekayaannya, dan menyombongkan harta bendanya.
7 Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
Sesungguhnya tak seorang pun dapat menyelamatkan saudaranya, atau membayar tebusannya kepada Allah.
8 Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
Apa pun yang diberikannya tak akan mencukupi; terlalu mahal harga tebusan nyawanya,
9 kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
agar ia terhindar dari mati dan dapat hidup selamanya.
10 Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
Tidak, ia akan melihat bahwa orang bijaksana pun mati. Orang dungu dan bodoh sama-sama binasa, dan meninggalkan hartanya bagi orang lain.
11 Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
Mereka akan tinggal di kuburan selama-lamanya; itulah kediaman mereka untuk seterusnya, walaupun dahulu mereka memiliki banyak tanah.
12 Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
Manusia tak dapat hidup terus dalam kemewahan; seperti binatang, ia pun akan binasa.
13 Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
Begitulah nasib orang yang mengandalkan dirinya, dan masa depan orang yang puas dengan perkataannya.
14 Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol h7585)
Seperti domba, mereka ditentukan untuk mati; maut akan menjadi gembala mereka. Pagi-pagi mereka dikalahkan oleh orang jujur; tubuh mereka segera membusuk di dunia orang mati, jauh dari kediaman yang mewah. (Sheol h7585)
15 Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol h7585)
Tetapi Allah akan membebaskan aku, Ia akan melepaskan aku dari kuasa maut. (Sheol h7585)
16 Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
Jangan takut kalau seorang menjadi kaya, dan hartanya bertambah banyak.
17 Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
Sebab waktu mati ia tak dapat membawa apa-apa, hartanya tak akan turun ke kubur bersama dia.
18 Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
Bahkan apabila seorang beruntung dalam hidupnya, dan disanjung-sanjung karena keberhasilannya,
19 iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
ia akan menyusul nenek moyangnya juga ke tempat yang gelap untuk selama-lamanya.
20 Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.
Manusia tak dapat terus hidup dalam kemewahan, seperti binatang, ia pun akan binasa.

< Masalimo 49 >