< Masalimo 49 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
Au maître-chantre. — Psaume des enfants de Coré. O peuples, écoutez tous; Prêtez tous l'oreille, habitants du monde,
2 anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
Enfants du peuple et enfants des grands, Le riche aussi bien que le pauvre!
3 Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
Ma bouche prononcera des paroles sages: Les pensées de mon coeur sont pleines de sens.
4 Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
Je prêterai l'oreille aux sentences qu'il m'inspire; J'expliquerai mon énigme au son de la harpe.
5 Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
Pourquoi aurais-je peur aux jours de l'infortune, Quand la méchanceté de mes adversaires m'environne?
6 Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
Ils se confient en leurs biens; Ils se glorifient de la grandeur de leurs richesses.
7 Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
Mais l'homme ne saurait racheter son frère, Ni payer à Dieu sa rançon:
8 Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
Le rachat d'une âme est trop cher; On ne saurait en payer le prix!
9 kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
Ils ne vivront pas toujours; Ils n'éviteront pas la vue du tombeau;
10 Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
Oui, ils le verront! Les sages meurent; Le fou et l'insensé périssent également, Et ils laissent leurs biens à d'autres.
11 Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
Ils pensent que leurs maisons dureront éternellement, Que leurs demeures subsisteront d'âge en âge; Et ils donnent leurs noms à leurs terres.
12 Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
Mais l'homme, même le plus opulent, n'a point de durée; Il est semblable aux bêtes vouées à la destruction.
13 Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
La voie qu'ils suivent est celle de la folie: Pourtant, ceux qui viennent après eux Approuvent leurs discours. (Pause)
14 Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol h7585)
Ils sont poussés vers le Séjour des morts comme un troupeau; La mort les conduit comme un berger. Quand vient le matin, les justes les foulent aux pieds; Leur beauté disparaîtra dans le tombeau! Ils n'auront pas d'autre demeure! (Sheol h7585)
15 Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol h7585)
Mais Dieu délivrera mon âme de l'étreinte du Séjour des morts; Car il me prendra sous sa garde. (Sheol h7585)
16 Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
Ne crains point, quand un homme s'enrichit, Quand l'opulence de sa maison s'accroît.
17 Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
Car, en mourant, il n'emportera rien; Son opulence ne le suivra pas dans la tombe.
18 Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
Tu as beau te proclamer heureux pendant ta vie, Ou t'attirer des louanges pour les joies que tu as en partage.
19 iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
Tu t'en iras pourtant vers la génération de tes pères. Qui ne reverront jamais la lumière.
20 Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.
L'homme, même le plus opulent, qui n'a point d'intelligence, Est semblable aux bêtes vouées à la destruction!

< Masalimo 49 >