< Masalimo 49 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
For the Chief Musician. A Psalm by the sons of Korah. Hear this, all you peoples. Listen, all you inhabitants of the world,
2 anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
both low and high, rich and poor together.
3 Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
My mouth will speak words of wisdom. My heart will utter understanding.
4 Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
I will incline my ear to a proverb. I will solve my riddle on the harp.
5 Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
Why should I fear in the days of evil, when iniquity at my heels surrounds me?
6 Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
Those who trust in their wealth, and boast in the multitude of their riches—
7 Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
none of them can by any means redeem his brother, nor give God a ransom for him.
8 Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
For the redemption of their life is costly, no payment is ever enough,
9 kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
that he should live on forever, that he should not see corruption.
10 Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
For he sees that wise men die; likewise the fool and the senseless perish, and leave their wealth to others.
11 Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
Their inward thought is that their houses will endure forever, and their dwelling places to all generations. They name their lands after themselves.
12 Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
But man, despite his riches, doesn’t endure. He is like the animals that perish.
13 Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
This is the destiny of those who are foolish, and of those who approve their sayings. (Selah)
14 Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol h7585)
They are appointed as a flock for Sheol. Death shall be their shepherd. The upright shall have dominion over them in the morning. Their beauty shall decay in Sheol, far from their mansion. (Sheol h7585)
15 Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol h7585)
But God will redeem my soul from the power of Sheol, for he will receive me. (Selah) (Sheol h7585)
16 Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
Don’t be afraid when a man is made rich, when the glory of his house is increased;
17 Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
for when he dies he will carry nothing away. His glory won’t descend after him.
18 Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
Though while he lived he blessed his soul— and men praise you when you do well for yourself—
19 iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
he shall go to the generation of his fathers. They shall never see the light.
20 Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.
A man who has riches without understanding, is like the animals that perish.

< Masalimo 49 >