< Masalimo 49 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
To the chief Musician. Of the sons of Korah. A Psalm. Hear this, all ye peoples; give ear, all inhabitants of the world:
2 anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
Both men of low and men of high degree, rich and poor alike.
3 Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
My mouth shall speak wisdom, and the meditation of my heart shall be of understanding:
4 Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
I will incline mine ear to a parable, I will open my riddle upon the harp.
5 Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
Wherefore should I fear in the days of adversity, [when] the iniquity of my supplanters encompasseth me? —
6 Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
They depend upon their wealth, and boast themselves in the abundance of their riches. ...
7 Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
None can by any means redeem his brother, nor give to God a ransom for him,
8 Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
(For the redemption of their soul is costly, and must be given up for ever, )
9 kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
That he should still live perpetually, [and] not see corruption.
10 Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
For he seeth that wise men die; all alike, the fool and the brutish perish, and they leave their wealth to others.
11 Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
Their inward thought is, that their houses are for ever, their dwelling-places from generation to generation: they call the lands after their own names.
12 Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
Nevertheless, man being in honour abideth not: he is like the beasts that perish.
13 Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
This their way is their folly, yet they that come after them delight in their sayings. (Selah)
14 Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol h7585)
Like sheep are they laid in Sheol: Death feedeth on them; and the upright shall have dominion over them in the morning; and their comeliness shall be for Sheol to consume, that there be no habitation for them. (Sheol h7585)
15 Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol h7585)
But God will redeem my soul from the power of Sheol: for he will receive me. (Selah) (Sheol h7585)
16 Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
Be not afraid when a man becometh rich, when the glory of his house is increased:
17 Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
For when he dieth, he shall carry nothing away; his glory shall not descend after him.
18 Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
Though he blessed his soul in his lifetime, — and men will praise thee when thou doest well to thyself, —
19 iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
It shall go to the generation of his fathers: they shall never see light.
20 Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.
Man that is in honour, and understandeth not, is like the beasts that perish.

< Masalimo 49 >