< Masalimo 49 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
Til Sangmesteren. Af Koras Sønner. En Salme. Hør det, alle Folkeslag, lyt til, al Verdens Folk,
2 anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
baade høj og lav, baade rig og fattig!
3 Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
Min Mund skal tale Visdom, mit Hjerte udgransker Indsigt;
4 Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
jeg bøjer mit Øre til Tankesprog, raader min Gaade til Strengeleg.
5 Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
Hvorfor skulle jeg frygte i de onde Dage, naar mine lumske Fjender omringer mig med Brøde,
6 Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
de, som stoler paa deres Gods og bryster sig af deres store Rigdom?
7 Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
Visselig, ingen kan købe sin Sjæl fri og give Gud en Løsesum
8 Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
— Prisen for hans Sjæl blev for høj, for evigt maatte han opgive det — saa han kunde blive i Live
9 kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
og aldrig faa Graven at se;
10 Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
nej, han skal se den; Vismænd dør, baade Daare og Taabe gaar bort. Deres Gods maa de afstaa til andre,
11 Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
deres Grav er deres Hjem for evigt, deres Bolig Slægt efter Slægt, om Godser end fik deres Navn.
12 Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
Trods Herlighed bliver Mennesket ikke, han er som Dyrene, der forgaar.
13 Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
Saa gaar det dem, der tror sig trygge, saa ender det for dem, deres Tale behager. (Sela)
14 Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol )
I Dødsriget drives de ned som Faar, deres Hyrde skal Døden være; de oprigtige træder paa dem ved Gry, deres Skikkelse gaar Opløsning i Møde, Dødsriget er deres Bolig. (Sheol )
15 Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol )
Men Gud udløser min Sjæl af Dødsrigets Haand, thi han tager mig til sig. (Sela) (Sheol )
16 Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
Frygt ej, naar en Mand bliver rig, naar hans Huses Herlighed øges;
17 Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
thi intet tager han med i Døden, hans Herlighed følger ham ikke.
18 Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
Priser han end i Live sig selv: »De lover dig for din Lykke!« —
19 iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
han vandrer til sine Fædres Slægt, der aldrig faar Lyset at skue.
20 Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.
Den, som lever i Herlighed, men uden Forstand, han er som Dyrene, der forgaar.