< Masalimo 49 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
Til Sangmesteren; af Koras Børn; en Psalme. Hører dette, alle Folkeslag! vender eders Øren hid, alle Verdens Indbyggere!
2 anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
baade ringe og høje, rige og fattige til Hobe!
3 Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
Min Mund udtaler Visdom og mit Hjertes Betænkning Forstand.
4 Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
Jeg vil bøje mit Øre til Ordsprog; jeg vil udlægge min mørke Tale til Harpe.
5 Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
Hvorfor skulde jeg frygte i de onde Dage, naar mine Efterstræberes Ondskab omgiver mig,
6 Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
de, som forlade sig paa deres Gods og rose sig af deres store Rigdom?
7 Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
Ingen Mand kan dog udløse en Broder, han kan ikke give Gud Løsepenge for ham.
8 Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
Thi deres Sjæls Genløsning vil koste meget og maa i Evighed opgives,
9 kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
saa at han skulde kunne leve hen bestandig uden at se Graven.
10 Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
Thi den vil han faa at se; de vise dø, Daaren og den ufornuftige omkomme tilsammen, og de efterlade deres Gods til andre.
11 Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
Deres inderste Tanker ere, at deres Huse skulle staa evindelig, deres Boliger fra Slægt til Slægt, de kalde deres Jorder op efter deres Navn.
12 Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
Dog har et Menneske, som er i Værdighed, ikke Bestand; han bliver lig Dyrene, som udryddes.
13 Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
Saa gaar det dem, som ere fulde af Selvtillid; dog love deres Efterkommere det med deres Mund. (Sela)
14 Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol )
De lægge sig i Dødsriget som Faar, Døden skal fortære dem og de oprigtige skulle regere over dem, naar Morgenen oprinder; og Dødsriget skal afslide deres Skikkelse, saa at den ingen Bolig har mere. (Sheol )
15 Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol )
Men Gud skal forløse min Sjæl af Dødsrigets Vold, thi han antager mig. (Sela) (Sheol )
16 Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
Frygt ikke, naar en Mand bliver rig, naar hans Hus's Herlighed bliver stor;
17 Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
thi han skal slet intet tage med sig, naar han dør, hans Herlighed skal ikke fare ned efter ham.
18 Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
Skønt han velsigner sin Sjæl, medens han lever, og man priser ham, fordi han gør sig til gode:
19 iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
Saa skal han dog komme til sine Fædres Slægt; i Evighed se de ikke Lyset.
20 Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.
Et Menneske, som er i Værdighed og ikke har Forstand, han bliver lig Dyrene, som udryddes.