< Masalimo 49 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
科辣黑後裔歌,用高音,交與樂官。 關於這事,請萬民都要靜聽,普世居民,請你們側耳細聽,
2 anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
不論貧富無分縉紳百姓,請你們都一一側耳聆聽。
3 Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
我的口要宣講智慧,我的心要思念哲理。
4 Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
我要側耳恭聽諺語,我要鼓琴解釋隱語。
5 Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
當陷害我者的毒謀圍我時,在我困厄的日期,我有何所懼?
6 Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
因為他們只知依恃財產的富足,他們只會誇耀自己金錢的豐裕;
7 Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
但是金錢不能使任何人得救,決不能把人的贖債還給天主,
8 Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
因為人命的贖債非常昂貴,任何金錢也決不足以贖回,
9 kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
不能使人生存久長,不能使人不見死亡。
10 Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
你看,智者死去,愚昧者也同樣沉淪,他們都將自己的財產遺留給別人。
11 Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
他們雖然曾以自己的名號,給一些地方命名,但是他們永久的住宅,萬代的居所卻是墳塋。
12 Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
人在富貴中絕不能久長,將與牲畜無異,同樣死亡。
13 Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
這就是自滿昏愚者的終途,這就是自誇幸運者的末路。
14 Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol )
他們就如羊群一般被人趕入深坑,死亡要牧放他們,義人要主宰他們。他們的容貌即刻色衰,陰間將是他們的住宅。 (Sheol )
15 Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol )
但是天主必救我靈脫離陰府,因為祂要把我接走。 (Sheol )
16 Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
不要嫉妒他人變成富翁,不要忌恨他人家產倍增;
17 Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
因為他死時什麼也不能帶走,他的財產也不能隨著他同去。
18 Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
他在生時雖我陶醉說:「只要你幸福,人必誇讚你。」
19 iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
他終要回去和他的祖先相逢,永永遠遠他再不能看到光明。
20 Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.
人在富貴中,不深思遠慮,將與牲畜無異,都要死去