< Masalimo 48 >

1 Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
Kora mma dwom. Awurade yɛ kɛseɛ na ɔsɛ nkamfo wɔ yɛn Onyankopɔn kuropɔn mu, ne bepɔ kronkron so.
2 Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
Kuropɔn no ɔsorokɔ yɛ fɛ, ɛyɛ ewiase nyinaa anigyedeɛ. Bepɔ Sion te sɛ Safon sorɔnsorɔmmea, Ɔhene Kɛseɛ no kuropɔn.
3 Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
Onyankopɔn te nʼabankɛsewa mu. Wada ne ho adi sɛ ɔyɛ nʼaban.
4 Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
Ɛberɛ a ahemfo yi boaa wɔn ho ano, na wɔtuu ɔsa bɔɔ mu no,
5 iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
wɔhunuu no ma ɛyɛɛ wɔn ahodwirie, na wɔde ehu dwaneeɛ.
6 Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
Nketenkete kyeree wɔn wɔ hɔ, ɔyea a ɛte sɛ ɔbaa a awoɔ aka no.
7 Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
Wosɛee wɔn sɛ Tarsis ahyɛn a apueeɛ mframa abɔ adwira wɔn.
8 Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
Sɛdeɛ yɛate no, saa ara na yɛahunu wɔ Otumfoɔ Awurade kuropɔn no mu, yɛn Onyankopɔn kuropɔn mu; Onyankopɔn ma ɛtim hɔ afebɔɔ.
9 Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
Wʼasɔredan no mu, Ao Onyankopɔn, na yɛdwene wo dɔ a ɛnsa da no ho,
10 Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
Ao Onyankopɔn, wʼayɛyie duru asase ano te sɛ wo din; tenenee ayɛ wo nsa nifa mu ma.
11 Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
Sion bepɔ di ahurisie, Yuda nkuraase no ani gye ɛsiane wʼatemmuo no enti.
12 Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
Nante Sion na twa ho hyia, kan nʼabantenten dodoɔ,
13 Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
dwene nʼafasuo ho yie, hwɛ nʼabankɛsewa no, na woaka ho asɛm akyerɛ nkyirimma.
14 Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.
Saa Onyankopɔn yi yɛ yɛn Onyankopɔn daa daa; mpo ɔbɛyɛ yɛn kwankyerɛfoɔ akɔsi awieeɛ.

< Masalimo 48 >