< Masalimo 48 >

1 Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
Koramma dwom. Awurade yɛ ɔkɛse na ɔsɛ nkamfo, wɔ yɛn Nyankopɔn kuropɔn mu, ne bepɔw kronkron so.
2 Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
Ne sorokɔ ma ɛyɛ fɛ, ɛyɛ wiase nyinaa anigyede. Bepɔw Sion te sɛ Safon sorɔnsorɔmmea, Ɔhenkɛse no kuropɔn.
3 Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
Onyankopɔn te nʼabankɛse mu wada ne ho adi sɛ ɔyɛ nʼabandennen.
4 Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
Bere a ahemfo yi boaa wɔn ho ano, na wotuu ɔsa bɔɔ mu no,
5 iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
wohuu no ma ɛyɛɛ wɔn ahodwiriw, na wɔde ehu guanee.
6 Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
Wɔbɔɔ huboa wɔ hɔ, ɔyaw a ɛte sɛ ɔbea a awo aka no.
7 Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
Wosɛe wɔn sɛ Tarsis ahyɛn a apuei mframa abɔ adwira wɔn.
8 Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
Sɛnea yɛate no, saa ara na yɛahu wɔ Asafo Awurade kuropɔn no mu, yɛn Nyankopɔn kuropɔn mu; Onyankopɔn ma etim hɔ afebɔɔ.
9 Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
Wʼasɔredan no mu; Ao, Onyankopɔn, na yɛdwene wo dɔ a enni huammɔ da no ho,
10 Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
Ao, Onyankopɔn, wʼayeyi du asase ano te sɛ wo din te; trenee ayɛ wo nsa nifa mu ma.
11 Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
Sion bepɔw di ahurusi, Yuda nkuraase no ani gye esiane wʼatemmu no nti.
12 Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
Nantew Sion na twa ho hyia, kan nʼabantenten dodow,
13 Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
dwene nʼafasu ho yiye, hwɛ nʼabankɛse no, na woaka ho asɛm akyerɛ nkyirimma.
14 Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.
Saa Onyankopɔn yi yɛ yɛn Nyankopɔn daa daa; ɔbɛyɛ yɛn kwankyerɛfo akosi awiei mpo. Wɔde ma dwonkyerɛfo.

< Masalimo 48 >