< Masalimo 48 >
1 Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
En Psalmvisa, Korah barnas. Stor är Herren, och högt berömd, uti vår Guds stad, på hans helga berg.
2 Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
Det berget Zion är såsom en skön telning, på hvilko hela landet tröster; på den sidone norrut ligger den stora Konungens stad.
3 Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
Gud är känd i hans palats, att han beskärmaren är.
4 Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
Ty si, Konungar äro församlade, och med hvarannan framdragne.
5 iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
De hafva förundrat sig, då de detta sågo; vordo häpne och omstörta.
6 Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
Bäfvande är dem der påkommet, ångest såsom ene födande qvinno.
7 Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
Du sönderbråkar skeppen i hafvet, igenom östanväder.
8 Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
Såsom vi hört hafve, så se vi det på Herrans Zebaoths stad, vår Guds stad. Gud håller honom vid magt evinnerliga. (Sela)
9 Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
Gud, vi förbide dina godhet i ditt tempel.
10 Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
Gud, såsom ditt Namn, så är ock ditt lof, allt intill verldenes ändar; din högra hand är full med rättfärdighet.
11 Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
Berget Zion fröjde sig, och Juda döttrar vare glada, för dina rätters skull.
12 Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
Går omkring Zion och beskåder det; täljer dess torn;
13 Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
Gifver granna akt uppå dess murar, och upphöjer dess palats; på det man derom må förkunna för efterkommanderna.
14 Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.
Ty denne Guden är vår Gud, alltid och evinnerliga; han förer oss såsom ungdomen.