< Masalimo 48 >

1 Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
Pesem in psalm naslednikom Koretovim. Velik je Gospod in hvaljen silno, v mestu Boga našega, na gori svetosti svoje:
2 Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
V lepoti kraja, veselji vse zemlje, na gori Sijonski, na severni strani v mestu kralja vélikega.
3 Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
Bog v dvorih njegovih spoznava se za grad.
4 Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
Ker, glej, sešli so se kralji, šli so vkup.
5 iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
Sami so videli, vkup so strmeli, zmedli so se, izbežali urno.
6 Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
Trepet jih je obšel tam, bolečina kakor porodnico.
7 Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
Z burjo razbijaš ladije morske.
8 Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
Kakor smo slišali, tako smo videli v mestu Gospoda vojnih krdél, v mestu Boga našega; Bog ga utrjuje na veke.
9 Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
Milost tvojo premišljamo, o Bog, sredi tvojega svetišča.
10 Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
Kakor ime tvoje, tako je slava tvoja noter do krajev zemlje; pravice je polna desnica tvoja.
11 Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
Veselí se naj gora Sijonska, radujejo se hčere Judove zavoljo sodeb tvojih.
12 Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
Obhajajte Sijon, in obdajajte ga; štejte stolpe njegove.
13 Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
Upirajte misli svoje na trdnjavo, povzdignite oči k dvorom njegovim, da oznanjate prihodnjemu rodu.
14 Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.
Ker ta je naš Bog na vedno večne čase; ta nas bode vodil noter do smrti.

< Masalimo 48 >