< Masalimo 48 >

1 Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
En sang, en salme; av Korahs barn. Stor er Herren og høilovet i vår Guds stad, på hans hellige berg.
2 Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
Fagert hever det sig, en glede for all jorden er Sions berg, det ytterste Norden, den store konges stad.
3 Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
Gud er i dens borger, han er blitt kjent som et fast vern.
4 Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
For se, kongene samlet sig, de drog frem tilsammen.
5 iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
De så, da blev de forferdet; de blev slått med redsel, flyktet i hast.
6 Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
Beven grep dem der, angst som hos en fødende kvinne.
7 Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
Ved østenvind knuste du Tarsis-skib.
8 Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
Likesom vi hadde hørt, så har vi nu sett det i Herrens, hærskarenes Guds stad, i vår Guds stad; Gud gjør den fast til evig tid. (Sela)
9 Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
Vi grunder, Gud, på din miskunnhet midt i ditt tempel.
10 Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
Som ditt navn, Gud, så er din pris inntil jordens ender; din høire hånd er full av rettferdighet.
11 Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
Sions berg gleder sig, Judas døtre fryder sig for dine dommers skyld.
12 Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
Gå omkring Sion og vandre rundt om det, tell dets tårn!
13 Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
Gi akt på dets voller, vandre gjennem dets borger, forat I kan fortelle derom til den kommende slekt.
14 Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.
For denne Gud er vår Gud evindelig og alltid; han skal føre oss ut over døden.

< Masalimo 48 >