< Masalimo 48 >

1 Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
Cantique. — Psaume des enfants de Coré. L'Éternel est grand et digne de toute louange. Dans la ville de notre Dieu, sur sa montagne sainte.
2 Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
Elle s'élève avec grâce, du côté du Septentrion, La montagne de Sion, joie de toute la terre: C'est la cité du grand roi.
3 Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
Dans ses palais, Dieu se révèle à nous Comme un rempart.
4 Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
Les rois s'étaient donné rendez-vous; Ils s'avançaient, ensemble.
5 iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
Ils virent Jérusalem; ils furent frappés d'étonnement, Terrifiés, mis en déroute.
6 Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
Soudain, ils furent saisis d'un tremblement, D'une angoisse pareille à celle de la femme qui enfante.
7 Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
Au souffle du vent de l'Orient, Tu brises les navires de Tarsis.
8 Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
Ce que nous avions entendu dire, nous l'avons vu Dans la ville de l'Éternel des armées, Dans la cité de notre Dieu: Dieu fera subsister Jérusalem à jamais. (Pause)
9 Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
Dieu, nous avons contemplé ta bonté Au milieu de ton temple.
10 Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
Ainsi que ton nom, ô Dieu, Ta louange retentit jusqu'aux extrémités de la terre. Ta main droite est pleine de justice.
11 Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
Que la montagne de Sion se réjouisse; Que les filles de Juda tressaillent d'allégresse, A cause de tes jugements.
12 Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
Faites le tour de Sion, parcourez son enceinte, Comptez ses tours,
13 Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
Considérez ses remparts, Examinez ses palais, Pour dire à la génération future:
14 Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.
«Ce Dieu est notre Dieu, pour toujours, à perpétuité; Il nous fera surmonter la mort!»

< Masalimo 48 >