< Masalimo 48 >

1 Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
Cantique de Psaume, des enfants de Coré. L'Eternel est grand, et fort louable en la ville de notre Dieu, en la montagne de sa Sainteté.
2 Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
Le plus beau de la contrée, la joie de toute la terre, c'est la montagne de Sion au fond de l'Aquilon; c'est la ville du grand Roi.
3 Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
Dieu est connu en ses palais pour une haute retraite.
4 Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
Car voici, les Rois s'étaient donné assignation, ils avaient passé outre tous ensemble.
5 iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
L'ont-ils vue? ils en ont été aussitôt étonnés; ils ont été tout troublés, ils s'en sont fuis à l'étourdie.
6 Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
Là le tremblement les a saisis, [et] une douleur comme de celle qui enfante.
7 Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
[Ils ont été chassés comme] par le vent d'Orient [qui] brise les navires de Tarsis.
8 Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
Comme nous l'avions entendu, ainsi l'avons-nous vu dans la ville de l'Eternel des armées, dans la ville de notre Dieu, laquelle Dieu maintiendra à toujours; (Sélah)
9 Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
Ô Dieu! nous avons entendu ta gratuité au milieu de ton Temple.
10 Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
Ô Dieu! tel qu'est ton Nom, telle [est] ta louange jusqu'aux bouts de la terre; ta droite est pleine de justice.
11 Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
La montagne de Sion se réjouira, et les filles de Juda auront de la joie, à cause de tes jugements.
12 Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
Environnez Sion, et l'entourez, [et] comptez ses tours.
13 Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
Prenez bien garde à son avant-mur, et considérez ses palais; afin que vous le racontiez à la génération à venir.
14 Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.
Car c'est le Dieu qui est notre Dieu à toujours et à perpétuité; il nous accompagnera jusques à la mort.

< Masalimo 48 >