< Masalimo 48 >

1 Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
A psalm of a canticle, for the sons of Core, on the second day of the week. Great is the Lord, and exceedingly to be praised in the city of our God, in his holy mountain.
2 Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
With the joy of the whole earth is mount Sion founded, on the sides of the north, the city of the great king.
3 Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
In her houses shall God be known, when he shall protect her.
4 Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
For behold the kings of the earth assembled themselves: they gathered together.
5 iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
So they saw, and they wondered, they were troubled, they were moved:
6 Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
Trembling took hold of them. There were pains as of a woman in labour.
7 Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
With a vehement wind thou shalt break in pieces the ships of Tharsis.
8 Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
As we have heard, so have we seen, in the city of the Lord of hosts, in the city of our God: God hath founded it for ever.
9 Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
We have received thy mercy, O God, in the midst of thy temple.
10 Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
According to thy name, O God, so also is thy praise unto the ends of the earth: thy right hand is full of justice.
11 Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
Let mount Sion rejoice, and the daughters of Juda be glad; because of thy judgments, O Lord.
12 Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
Surround Sion, and encompass her: tell ye in her towers.
13 Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
Set your hearts on her strength; and distribute her houses, that ye may relate it in another generation.
14 Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.
For this is God, our God unto eternity, and for ever and ever: he shall rule us for evermore.

< Masalimo 48 >