< Masalimo 48 >
1 Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
(En sang. En salme af Koras sønner.) Stor og højlovet er vor Gud i sin Stad.
2 Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
Smukt løfter sig hans hellige Bjerg, al Jordens Fryd, Zions Bjerg i det højeste Nord, den store Konges By.
3 Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
Som Værn gjorde Gud sig kendt i dens Borge.
4 Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
Thi Kongerne samlede sig, rykked frem tilsammen;
5 iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
de så og tav på Stedet, flyed i Angst,
6 Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
af Rædsel grebes de brat, af Veer som en, der føder.
7 Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
Med Østenstormen knuser du Tarsisskibe.
8 Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
Som vi havde hørt det, så vi det selv i Hærskarers HERREs By, i vor Guds By; til evig Tid lader Gud den stå. (Sela)
9 Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
I din Helligdom tænker vi, Gud, på din Miskundhed;
10 Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
som dit Navn så lyder din Pris til Jordens Grænser. Din højre er fuld af Retfærd,
11 Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
Zions Bjerg fryder sig, Judas Døtre jubler over dine Domme.
12 Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
Drag rundt om Zion, gå rundt og tæl dets Tårne,
13 Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
læg Mærke til dets Ringmur, så gennem dets Borge, at I kan melde Slægten, der
14 Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.
kommer: Sådan er Gud, vor Gud for evigt og altid, han skal lede os.