< Masalimo 47 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Ombani mʼmanja, inu anthu onse; fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
För sångmästaren; av Koras söner; en psalm.
2 Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba; Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
Klappen i händerna, alla folk, höjen jubel till Gud med fröjderop.
3 Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu; anayika anthu pansi pa mapazi athu.
Ty HERREN är den Högste, fruktansvärd är han, en stor konung över hela jorden.
4 Iye anatisankhira cholowa chathu, chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda. (Sela)
Han tvingar folk under oss och folkslag under våra fötter.
5 Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe, Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
Han utväljer åt oss vår arvedel, Jakobs, hans älskades, stolthet. (Sela)
6 Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando; imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
Gud har farit upp under jubel, HERREN, under basuners ljud.
7 Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani Iye salimo la matamando.
Lovsjungen Gud, lovsjungen; lovsjungen vår konung, lovsjungen.
8 Mulungu akulamulira mitundu ya anthu; Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
Ty Gud är konung över hela jorden; lovsjungen honom med en sång.
9 Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana monga anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu; Iye wakwezedwa kwakukulu.
Gud är nu konung över hedningarna, Gud har satt sig på sin heliga tron. Folkens ypperste hava församlat sig till att bliva ett Abrahams Guds folk. Ty Gud tillhöra de som äro jordens sköldar; högt är han upphöjd.

< Masalimo 47 >