< Masalimo 47 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Ombani mʼmanja, inu anthu onse; fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
¡Aplaudan, pueblos todos! dejando que tus voces suban a Dios con alegría.
2 Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba; Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
Porque el Señor Altísimo es temido; él es un gran Rey sobre toda la tierra.
3 Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu; anayika anthu pansi pa mapazi athu.
El someterá los pueblos debajo de nosotros y a las naciones debajo de nuestros pies.
4 Iye anatisankhira cholowa chathu, chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda. (Sela)
Él nos dará nuestra herencia, la gloria de Jacob que es querido por él. (Selah)
5 Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe, Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
Dios ha subido con un clamor alegre, el Señor con el sonido del cuerno.
6 Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando; imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
Alaben a Dios, hagan canciones de alabanza; dale alabanzas a nuestro Rey, haz canciones de alabanza.
7 Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani Iye salimo la matamando.
Porque Dios es el Rey de toda la tierra; hacer salmos de alabanza.
8 Mulungu akulamulira mitundu ya anthu; Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
Dios es el gobernante sobre las naciones; Dios está en el alto puesto en su santo trono.
9 Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana monga anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu; Iye wakwezedwa kwakukulu.
Los príncipes de los pueblos se juntaron con el pueblo del Dios de Abraham; porque los poderes de la tierra son de Dios: él es muy exaltado.

< Masalimo 47 >