< Masalimo 47 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Ombani mʼmanja, inu anthu onse; fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
Todos los pueblos batid las manos: clamád a Dios con voz de alegría.
2 Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba; Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
Porque Jehová es sublime y temeroso: Rey grande sobre toda la tierra.
3 Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu; anayika anthu pansi pa mapazi athu.
Él someterá a los pueblos debajo de nosotros, y a las naciones debajo de nuestros pies.
4 Iye anatisankhira cholowa chathu, chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda. (Sela)
El nos eligirá nuestras heredades; la hermosura de Jacob, al cual amó. (Selah)
5 Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe, Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
Subió Dios con júbilo, Jehová con voz de trompeta.
6 Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando; imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
Cantád a Dios, cantád; cantád a nuestro Rey, cantád.
7 Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani Iye salimo la matamando.
Porque el Rey de toda la tierra es Dios: cantád entendiendo.
8 Mulungu akulamulira mitundu ya anthu; Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
Reinó Dios sobre las naciones: Dios se asentó sobre su santo trono.
9 Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana monga anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu; Iye wakwezedwa kwakukulu.
Los príncipes de los pueblos se juntaron al pueblo del Dios de Abraham: porque de Dios son los escudos de la tierra; él es muy ensalzado.