< Masalimo 47 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Ombani mʼmanja, inu anthu onse; fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
Para el músico principal. Un salmo de los hijos de Coré. Oh, aplaudid todas las naciones. ¡Grita a Dios con voz de triunfo!
2 Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba; Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
Porque Yahvé el Altísimo es imponente. Es un gran Rey sobre toda la tierra.
3 Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu; anayika anthu pansi pa mapazi athu.
Él somete a las naciones bajo nosotros, y pueblos bajo nuestros pies.
4 Iye anatisankhira cholowa chathu, chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda. (Sela)
Él elige nuestra herencia por nosotros, la gloria de Jacob a quien amó. (Selah)
5 Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe, Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
Dios ha subido con un grito, Yahvé con el sonido de una trompeta.
6 Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando; imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
¡Cantad alabanzas a Dios! ¡Canten alabanzas! ¡Cantad alabanzas a nuestro Rey! ¡Cantad alabanzas!
7 Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani Iye salimo la matamando.
Porque Dios es el Rey de toda la tierra. Canta alabanzas con comprensión.
8 Mulungu akulamulira mitundu ya anthu; Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
Dios reina sobre las naciones. Dios se sienta en su santo trono.
9 Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana monga anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu; Iye wakwezedwa kwakukulu.
Los príncipes de los pueblos están reunidos, el pueblo del Dios de Abraham. Porque los escudos de la tierra pertenecen a Dios. Es muy exaltado.

< Masalimo 47 >