< Masalimo 47 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Ombani mʼmanja, inu anthu onse; fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
Salmo, [dato] al Capo de' Musici, de' figliuoli di Core BATTETEVI a palme, o popoli tutti; Giubilate a Dio con voce di trionfo.
2 Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba; Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
Perciocchè il Signore [è] l'Altissimo, il Tremendo, Gran Re sopra tutta la terra.
3 Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu; anayika anthu pansi pa mapazi athu.
Egli ridurrà i popoli sotto noi, E la nazioni sotto i nostri piedi.
4 Iye anatisankhira cholowa chathu, chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda. (Sela)
Egli ci ha scelta la nostra eredità, La gloria di Giacobbe, il quale egli ama. (Sela)
5 Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe, Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
Iddio è salito con giubilo, Il Signore [è salito] con suono di trombe.
6 Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando; imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
Salmeggiate a Dio, salmeggiate; Salmeggiate al Re nostro, salmeggiate.
7 Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani Iye salimo la matamando.
Perciocchè Iddio [è] Re di tutta la terra; Salmeggiate maestrevolmente
8 Mulungu akulamulira mitundu ya anthu; Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
Iddio regna sopra le genti: Iddio siede sopra il trono della sua santità.
9 Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana monga anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu; Iye wakwezedwa kwakukulu.
I principi de' popoli si son raunati insieme; Il popolo dell'Iddio d'Abrahamo, Perciocchè a Dio [appartengono] gli scudi della terra; Egli è grandemente esaltato.

< Masalimo 47 >