< Masalimo 47 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Ombani mʼmanja, inu anthu onse; fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
[Dem Vorsänger. Von den Söhnen Korahs, ein Psalm.] Ihr Völker alle, klatschet in die Hände! Jauchzet Gott mit Jubelschall!
2 Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba; Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
Denn Jehova, der Höchste, ist furchtbar, ein großer König über die ganze Erde.
3 Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu; anayika anthu pansi pa mapazi athu.
Er unterwarf uns die Völker, und die Völkerschaften unter unsere Füße.
4 Iye anatisankhira cholowa chathu, chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda. (Sela)
Er erwählte für uns unser Erbteil, den Stolz Jakobs, den er geliebt hat. (Sela)
5 Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe, Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
Gott ist emporgestiegen unter Jauchzen, Jehova unter Posaunenschall.
6 Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando; imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
Singet Gott Psalmen, [Eig. Singspielet] singet Psalmen; singet Psalmen unserem König, singet Psalmen!
7 Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani Iye salimo la matamando.
Denn Gott ist König der ganzen Erde; singet Psalmen mit Einsicht! [Eig. Singet Maskil. S. die Anm. zu Ps. 32, Überschrift]
8 Mulungu akulamulira mitundu ya anthu; Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
Gott regiert über die Nationen; Gott hat sich auf den Thron seiner Heiligkeit gesetzt.
9 Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana monga anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu; Iye wakwezedwa kwakukulu.
Die Edlen der Völker haben sich versammelt und das Volk [O. als ein Volk] des Gottes Abrahams; denn die Schilde [d. h. die Fürsten, die Schirmherren] der Erde sind Gottes; er ist sehr erhaben.

< Masalimo 47 >