< Masalimo 47 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Ombani mʼmanja, inu anthu onse; fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
Pour la fin, pour les fils de Coré, psaume. Nations, battez toutes des mains: poussez des cris de joie vers Dieu, avec une voix d’exultation,
2 Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba; Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
Parce que le Seigneur est très élevé et terrible: c’est un grand roi sur toute la terre.
3 Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu; anayika anthu pansi pa mapazi athu.
Il nous a assujetti des peuples, et a mis des nations sous nos pieds.
4 Iye anatisankhira cholowa chathu, chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda. (Sela)
Il a choisi en nous son héritage, la beauté de Jacob qu’il a aimée.
5 Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe, Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
Dieu est monté au milieu des acclamations de joie, et le Seigneur au son de la trompette.
6 Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando; imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
Chantez notre Dieu, chantez: chantez notre Roi, chantez.
7 Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani Iye salimo la matamando.
Parce que le roi de toute la terre est Dieu: chantez avec sagesse.
8 Mulungu akulamulira mitundu ya anthu; Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
Dieu régnera sur les nations: Dieu est assis sur son trône saint.
9 Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana monga anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu; Iye wakwezedwa kwakukulu.
Des princes de peuples se sont réunis au Dieu d’Abraham; parce que les dieux puissants de la terre ont été extraordinairement élevés.