< Masalimo 47 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Ombani mʼmanja, inu anthu onse; fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
O clap your hands, all you people; shout to God with the voice of triumph.
2 Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba; Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
For the LORD most high is terrible; he is a great King over all the earth.
3 Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu; anayika anthu pansi pa mapazi athu.
He shall subdue the people under us, and the nations under our feet.
4 Iye anatisankhira cholowa chathu, chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda. (Sela)
He shall choose our inheritance for us, the excellency of Jacob whom he loved. (Selah)
5 Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe, Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
God is gone up with a shout, the LORD with the sound of a trumpet.
6 Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando; imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
Sing praises to God, sing praises: sing praises to our King, sing praises.
7 Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani Iye salimo la matamando.
For God is the King of all the earth: sing you praises with understanding.
8 Mulungu akulamulira mitundu ya anthu; Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
God reigns over the heathen: God sits on the throne of his holiness.
9 Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana monga anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu; Iye wakwezedwa kwakukulu.
The princes of the people are gathered together, even the people of the God of Abraham: for the shields of the earth belong to God: he is greatly exalted.