< Masalimo 47 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Ombani mʼmanja, inu anthu onse; fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
Unto the end. A Psalm for the sons of Korah. All nations, clap your hands. Shout joyfully to God with a voice of exultation.
2 Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba; Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
For the Lord is exalted and terrible: a great King over all the earth.
3 Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu; anayika anthu pansi pa mapazi athu.
He has subjected the peoples to us and subdued the nations under our feet.
4 Iye anatisankhira cholowa chathu, chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda. (Sela)
He has chosen us for his inheritance: the splendor of Jacob, whom he has loved.
5 Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe, Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
God ascends with jubilation, and the Lord with the voice of the trumpet.
6 Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando; imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
Sing psalms to our God, sing psalms. Sing psalms to our King, sing psalms.
7 Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani Iye salimo la matamando.
For God is the King of all the earth. Sing psalms wisely.
8 Mulungu akulamulira mitundu ya anthu; Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
God will reign over the peoples. God sits upon his holy throne.
9 Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana monga anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu; Iye wakwezedwa kwakukulu.
The leaders of the peoples have been gathered together by the God of Abraham. For the strong gods of the earth have been exceedingly exalted.

< Masalimo 47 >