< Masalimo 46 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Nyimbo ya anamwali. Mulungu ndiye kothawira kwathu ndi mphamvu yathu, thandizo lopezekeratu pa nthawi ya mavuto.
Koramma dwom. Wɔto no “alamot” sanku nne so. Onyankopɔn ne yɛn guankɔbea ne yɛn ahoɔden, amanehunu mu boafo a ɔwɔ hɔ bere biara.
2 Nʼchifukwa chake sitidzaopa ngakhale dziko lapansi lisunthike, ngakhale mapiri agwe pakati pa nyanja,
Enti sɛ asase ani dan butuw, na mmepɔw tutu kogu po ase a, yɛrensuro,
3 ngakhale madzi ake atakokoma ndi kuchita thovu, ngakhale mapiri agwedezeke ndi kukokoma kwake.
sɛ po bɔ asorɔkye na ehuru na ɛma nkoko wosow mpo a, yɛrensuro.
4 Kuli mtsinje umene njira zake za madzi zimasangalatsa mzinda wa Mulungu, malo oyera kumene Wammwambamwamba amakhalako.
Asuten bi wɔ hɔ a ne nsuwansuwa de anigye ba Onyankopɔn kuropɔn mu, beae kronkron a Ɔsorosoroni no te.
5 Mulungu ali mʼkati mwake, iwo sudzagwa; Mulungu adzawuthandiza mmawa.
Onyankopɔn te kuropɔn no mu, na ɔrenhwe ase; Onyankopɔn bɛboa no anɔpahema.
6 Mitundu ikupokosera, mafumu akugwa; Iye wakweza mawu ake, dziko lapansi likusungunuka.
Amanaman yɛ hoo, na ahenni hwehwe ase; ɔma ne nne so ma asase nan.
7 Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife, Mulungu wa Yakobo ndi linga lathu.
Asafo Awurade ka yɛn ho. Yakob Nyankopɔn yɛ yɛn aban.
8 Bwerani kuti mudzaone ntchito za Yehova, chiwonongeko chimene wachibweretsa pa dziko lapansi.
Bra bɛhwɛ Awurade nnwuma, ɔsɛe a ɔde aba asase no so.
9 Iye amathetsa nkhondo ku malekezero a dziko lapansi; Iye amathyola uta ndi kupindapinda mkondo; amatentha zishango ndi moto.
Ɔma akodi gyae kosi asase ano. Obubu agyan mu na ɔsɛe peaw; ɔde ogya hyew nkatabo.
10 Iye akuti, “Khala chete, ndipo dziwa kuti ndine Mulungu; ndidzakwezedwa pakati pa mitundu ya anthu; ine ndidzakwezedwa mʼdziko lapansi.”
Monyɛ komm na munhu sɛ me ne Onyankopɔn; wɔbɛma me so wɔ amanaman no mu, wɔbɛma me so wɔ asase so.
11 Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife, Mulungu wa Yakobo ndi linga lathu.
Asafo Awurade ka yɛn ho; Yakob Nyankopɔn yɛ yɛn aban. Wɔde ma dwonkyerɛfo.

< Masalimo 46 >