< Masalimo 46 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Nyimbo ya anamwali. Mulungu ndiye kothawira kwathu ndi mphamvu yathu, thandizo lopezekeratu pa nthawi ya mavuto.
O KE Akua ka puuhonua a me ka ikaika o kakou, He kokua kokoke loa i ka popilikia ana.
2 Nʼchifukwa chake sitidzaopa ngakhale dziko lapansi lisunthike, ngakhale mapiri agwe pakati pa nyanja,
Nolaila, aole makou e makau ke laweia'ku ka honua, A ke haliia'ku na mauna iwaena konu o ka moana;
3 ngakhale madzi ake atakokoma ndi kuchita thovu, ngakhale mapiri agwedezeke ndi kukokoma kwake.
Ke halulu hoi kona mau wai me ke kupikipikio, Ke haalulu hoi na mauna i kona hookiekie ana. (Sila)
4 Kuli mtsinje umene njira zake za madzi zimasangalatsa mzinda wa Mulungu, malo oyera kumene Wammwambamwamba amakhalako.
He muliwai nae i hoohauoli ai kona mau waikahe i ke kulanakauhale o ke Akua, I kahi hoano o na halelewa o ka mea kiekie loa.
5 Mulungu ali mʼkati mwake, iwo sudzagwa; Mulungu adzawuthandiza mmawa.
O ke Akua ka iwaena konu ona, Aole ia e hoonauweweia: E kokua mai ke Akua ia ia i ka wehe ana'e o ke alaula.
6 Mitundu ikupokosera, mafumu akugwa; Iye wakweza mawu ake, dziko lapansi likusungunuka.
Kupikipikio ae la na lahuikanaka, Nauwewe ae la na aupuni: Haawi mai la oia i kona leo, Hehee iho la ka honua.
7 Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife, Mulungu wa Yakobo ndi linga lathu.
O Iehova Sabaota, oia me kakou: O ko Iakoba Akua ko kakou wahi e malu ai. (Sila)
8 Bwerani kuti mudzaone ntchito za Yehova, chiwonongeko chimene wachibweretsa pa dziko lapansi.
E hele mai e nana i na hana a Iehova, I kona hooneoneo ana ma ka honua.
9 Iye amathetsa nkhondo ku malekezero a dziko lapansi; Iye amathyola uta ndi kupindapinda mkondo; amatentha zishango ndi moto.
Ke hooki mai nei oia i na kaua a i ka welau o ka honua; Uhaki oia i ke kakaka, Oki pu hoi oia i ka ihe a kaawale; Hoopau hoi oia i ke kaakaua i ke ahi.
10 Iye akuti, “Khala chete, ndipo dziwa kuti ndine Mulungu; ndidzakwezedwa pakati pa mitundu ya anthu; ine ndidzakwezedwa mʼdziko lapansi.”
E noho malie, a e ike hoi e, Owau no ke Akua. E hapaiia au iwaena o na lahuikanaka; E hookiekieia hoi au ma ka honua.
11 Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife, Mulungu wa Yakobo ndi linga lathu.
O Iehova Sabaota oia me kakou; O ko Iakoba Akua ko kakou wahi e malu ai. (Sila)

< Masalimo 46 >