< Masalimo 45 >
1 Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati. Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu; lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.
Для дириґента хору. На „Лілеї“. Синів Коре́євих. Псалом навча́льний. Пісня любови. Моє серце брини́ть добрим словом, проказую я: Для Царя мої тво́ри, мій язик — мов перо скоропи́сця!
2 Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika, popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.
Ти кращий від лю́дських синів, в Твоїх устах розлита краса́ та добро́, тому благослови́в Бог навіки Тебе.
3 Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu; mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.
Прив'яжи до стегна́ Свого, Сильний, Свого меча, красу́ Свою́ та вели́чність Свою́,
4 Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo; dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.
і в вели́чності Своїй сідай, та й ве́рхи помчися за справи правди, і ла́гідности та справедливости, — і на́вчить Тебе страшних чинів прави́ця Твоя́!
5 Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu, mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.
Твої стрі́ли наго́стрені, — а від них під Тобою наро́ди попа́дають, — у серце Царськи́х ворогів.
6 Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi; ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.
Престол Твій, о Боже, на вічні віки́, берло правди — берло Царства Твого́.
7 Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.
Ти полюбив справедливість, а беззако́ння знена́видів, тому́ намасти́в Тебе Бог, Твій Бог, оливою радости понад друзів Твоїх.
8 Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya; kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.
Ми́ро, ало́е й кассі́я — всі ша́ти Твої, а з палат із слоно́вої кости — струни Тебе звесели́ли.
9 Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka; ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.
Серед ска́рбів Твоїх — царські до́чки, по правиці Твоїй стала цариця в офі́рському щирому золоті.
10 Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu; iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.
Слухай, до́чко, й побач, і нахили своє ухо, — і забудь свій наро́д і дім батька свого́!
11 Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako; mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.
А Цар буде жадати твоєї краси́, бо Він — твій Госпо́дь, а ти до землі Йому кланяйся.
12 Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso, amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.
А Ти́рська дочка́ прийде з да́ром, будуть благати тебе найбагатші з наро́ду.
13 Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake, chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.
Вся оздо́ба царсько́ї дочки́ — усере́дині, шата ж її погапто́вана золотом.
14 Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu; anamwali okhala naye akumutsatira ndipo abweretsedwa kwa inu.
У ша́ти гапто́вані вбрану прова́дять її до Царя, за нею дівча́та, подру́ги її, до Тебе прова́джені.
15 Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo; akulowa mʼnyumba yaufumu.
Провадять їх з ра́дощами та поті́хою, — у палату царську́ вони ві́йдуть.
16 Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako; udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.
Замість батькі́в Твоїх бу́дуть сини́ Твої, — їх по ці́лій землі Ти поставиш воло́дарями.
17 Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse; choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.
Я буду Ім'я́ Твоє зга́дувати по всіх поколіннях, тому́ то наро́ди по вічні віки Тебе сла́вити будуть!