< Masalimo 45 >
1 Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati. Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu; lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.
Para el músico jefe. Con la música de “Los Lirios”. Una contemplación de los hijos de Coré. Una canción de boda. Mi corazón rebosa de un tema noble. Recito mis versos para el rey. Mi lengua es como la pluma de un hábil escritor.
2 Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika, popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.
Tú eres el más excelente de los hijos de los hombres. La gracia ha ungido tus labios, por eso Dios te ha bendecido para siempre.
3 Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu; mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.
Pon tu espada en el muslo, oh poderoso, en tu esplendor y tu majestad.
4 Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo; dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.
En tu majestuosidad cabalga victorioso en nombre de la verdad, la humildad y la rectitud. Deja que tu mano derecha muestre acciones asombrosas.
5 Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu, mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.
Tus flechas son afiladas. Las naciones caen bajo ti, con flechas en el corazón de los enemigos del rey.
6 Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi; ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.
Tu trono, Dios, es eterno y para siempre. Un cetro de equidad es el cetro de tu reino.
7 Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.
Has amado la justicia y odiado la maldad. Por eso Dios, tu Dios, te ha ungido con el aceite de la alegría por encima de tus compañeros.
8 Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya; kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.
Todos tus vestidos huelen a mirra, áloe y casia. De los palacios de marfil los instrumentos de cuerda te han alegrado.
9 Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka; ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.
Las hijas de los reyes están entre tus mujeres honorables. A su derecha la reina se encuentra en oro de Ophir.
10 Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu; iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.
Escucha, hija, considera y vuelve tu oído. Olvídate de tu propia gente, y también de la casa de tu padre.
11 Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako; mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.
Así el rey deseará tu belleza, honradlo, pues es vuestro señor.
12 Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso, amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.
La hija de Tiro viene con un regalo. Los ricos del pueblo suplican su favor.
13 Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake, chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.
La princesa en su interior es toda una gloria. Su ropa está entretejida con oro.
14 Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu; anamwali okhala naye akumutsatira ndipo abweretsedwa kwa inu.
Será llevada al rey en una obra bordada. Las vírgenes, sus compañeras que la siguen, serán traídas a ti.
15 Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo; akulowa mʼnyumba yaufumu.
Con alegría y regocijo serán conducidos. Entrarán en el palacio del rey.
16 Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako; udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.
Sus hijos ocuparán el lugar de sus padres. Los harás príncipes en toda la tierra.
17 Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse; choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.
haré que tu nombre sea recordado en todas las generaciones. Por eso los pueblos te darán gracias por los siglos de los siglos.