< Masalimo 45 >
1 Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati. Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu; lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.
Kumqondisi wokuhlabela. Njengengoma ethi “Izimbali.” Ihubo lamaDodana kaKhora. Ingoma yomtshado. Inhliziyo yami iyagubhazela ngendaba enkulu nxa ngivuma inkondlo yami ngiyihayela inkosi; ulimi lwami lusiba lomlobi ololwazi.
2 Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika, popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.
Uyilikhwa lamakhwa emadodeni wonke lezindebe zakho ziconjwe kuhle ngobunono, njengalokhu uNkulunkulu ekubusisile lanininini.
3 Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu; mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.
Hloma inkemba yakho okhalweni, wena omkhulu; zembathise ngokukhazimula langobukhosi.
4 Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo; dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.
Usebukhosini bakho khwela enqoleni ulokunqoba umele iqiniso lokuzithoba lokulunga; akuthi isandla sakho sokunene senze izimanga.
5 Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu, mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.
Akuthi imitshoko yakho ecijileyo icibe inhliziyo zezitha zenkosi; akuthi izizwe ziwe ngaphansi kwezinyawo zakho.
6 Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi; ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.
Isihlalo sakho sobukhosi, Oh Nkulunkulu, sizakuma nini lanini; intonga yokwahlulela okulungileyo izakuba yintonga yombuso wakho.
7 Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.
Uyakuthanda ukulunga njalo uyabuzonda ububi; ngakho uNkulunkulu, uNkulunkulu wakho usekubeke ngaphezu kwabakhula bakho ngokukugcoba ngamafutha entokozo.
8 Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya; kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.
Zonke izembatho zakho ziqholiwe ngemure, langenhlaba langekhasiya; ezigodlweni eziceciswe ngempondo zendlovu kuqhamuka inhlokomo yeziginci ekuthokozisayo.
9 Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka; ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.
Amadodakazi amakhosi akhona kanye labanye abesifazane abahloniphekayo; kwesokunene sakho ngumlobokazi wesikhosini oceciswe ngegolide lase-Ofiri.
10 Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu; iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.
Lalela, ndodakazi, nanzelela uvule indlebe; khohlwa abakini, lendlu yakwenu.
11 Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako; mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.
Inkosi iyaphelelwa ngobuhle bakho; yihloniphe, ngoba iyinkosi yakho.
12 Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso, amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.
Indodakazi yaseThire izakuza lesipho, amadoda anothileyo azazincengela kuwe.
13 Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake, chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.
Ngaphakathi exhibeni layo inkosazana yibucwazicwazi; isembatho sayo sicecisiwe ngegolide.
14 Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu; anamwali okhala naye akumutsatira ndipo abweretsedwa kwa inu.
Isiwa enkosini yembethe izivunulo ezelukiweyo; abakhaphi bayo bayayilandela balethwe kuwe.
15 Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo; akulowa mʼnyumba yaufumu.
Bangeniswa lapho ngentokozo lenjabulo; bangena esigodlweni senkosi.
16 Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako; udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.
Amadodana enu azathatha isikhundla saboyihlo; lizawenza abe ngamakhosana elizweni lonke.
17 Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse; choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.
Ibizo lakho ngizalenza likhunjulwe kokuphela yizizukulwane zonke; yikho-ke izizwe zizakudumisa nini lanini.