< Masalimo 45 >

1 Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati. Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu; lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.
Nzembo ya bolingo oyo bana ya Kore bayembaki. Wuta na buku ya mokambi ya bayembi. Eyembamaki na lindanda oyo babengaka Lisi. Motema na ngai etondi na maloba kitoko. Namilobeli: Nakotatola misala na ngai mpo na mokonzi. Tika ete lolemo na ngai ezala lokola ekomeli ya mokomi ya mayele.
2 Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika, popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.
Oleki bato nyonso na kitoko, mpe bibebu na Yo ebimisaka ngolu; yango wana Nzambe apambola Yo mpo na libela.
3 Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu; mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.
Elombe ya bitumba, kanga mopanga na loketo na Yo! Lata lokumu mpe kongenga.
4 Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo; dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.
Kati na kongenga na Yo, zala molongi, mata na shar na Yo, telema mpo na solo, mpo na komikitisa, mpe mpo na bosembo; tika ete loboko na Yo ya mobali esala misala minene.
5 Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu, mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.
Tika ete makonga na Yo ya minu etobola mitema ya banguna ya mokonzi; tika ete bikolo ekweya na se ya matambe na Yo.
6 Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi; ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.
Nzambe, Kiti ya Bokonzi na Yo ekowumela seko na seko; lingenda ya bokonzi na Yo ezali mpo na bosembo.
7 Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.
Olingaka bosembo mpe oyinaka mabe; yango wana, oh Nzambe, Nzambe na Yo apakoli Yo mafuta ya esengo, asepeli na Yo koleka baninga na Yo.
8 Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya; kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.
Bilamba na Yo nyonso ezali kolumba solo kitoko ya malasi ya mire, ya aloe mpe ya kaneli; wuta na bandako minene oyo ebongisama na pembe ya nzoko, mandanda ezali kosepelisa Yo.
9 Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka; ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.
Bana basi ya bakonzi bazali kati na basi ya lokumu; mwasi ya mokonzi azali na ngambo ya loboko na Yo ya mobali, alati biloko ya wolo ya Ofiri.
10 Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu; iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.
Mwana na ngai ya mwasi, tala mpe yoka; bosana bato na yo mpe ndako ya tata na yo.
11 Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako; mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.
Mokonzi asepeli na kitoko na yo; lokola azali nkolo na yo, gumbama liboso na ye.
12 Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso, amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.
Tiri, mboka kitoko, bato oyo baleki na bozwi kati na bato bakomemela yo bakado mpo ete olinga bango.
13 Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake, chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.
Mwana mwasi ya mokonzi azali kongenga na kitoko kati na ndako ya mokonzi, alati elamba batonga wolo.
14 Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu; anamwali okhala naye akumutsatira ndipo abweretsedwa kwa inu.
Alati bilamba batonga bililingi kitoko na basinga, mpe bamemi ye epai ya mokonzi. Bamemi mpe balingami na ye epai na yo, bilenge basi oyo batambolaka elongo na ye.
15 Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo; akulowa mʼnyumba yaufumu.
Bamemi bango na nsayi mpe na esengo; bakoti na ndako ya mokonzi.
16 Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako; udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.
Bana na yo ya mibali bakozwa esika ya bakoko na bango; okotia bango bakambi kati na mokili mobimba.
17 Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse; choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.
Nakosala ete bikeke nyonso ebosana kombo na yo te. Boye bikolo nyonso ekosanzola Yo tango nyonso, seko na seko.

< Masalimo 45 >