< Masalimo 45 >

1 Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati. Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu; lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.
Au maître-chantre. — Sur «les lis.» — Hymne des enfants de Goré. — Cantique nuptial. De mon coeur débordent des paroles excellentes. Je me dis: «Mon oeuvre est pour le roi!» Ma langue sera comme la plume d'un habile écrivain.
2 Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika, popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.
Tu es beau, plus beau qu'aucun des fils des hommes. La grâce est répandue sur tes lèvres; C'est pourquoi Dieu t'a béni à jamais.
3 Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu; mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.
Vaillant guerrier, ceins sur tes flancs ton épée, — Ta parure et ta magnificence,
4 Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo; dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.
Oui, ta magnificence! — Cours à la victoire, monte sur ton char. Pour le triomphe de la vérité, de la clémence et de la justice. Que ta main droite te fasse accomplir des exploits redoutables!
5 Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu, mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.
Tes flèches sont aiguës: Elles feront tomber les peuples sous tes pieds; Elles frapperont au coeur les ennemis du roi!
6 Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi; ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.
Ton trône, ô Dieu, est établi pour toujours, à perpétuité; Le sceptre de ta royauté est un sceptre de justice.
7 Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.
Tu aimes la justice et tu hais la méchanceté; C'est pourquoi, ô Dieu, ton Dieu t'a oint D'une huile d'allégresse, de préférence à tous tes égaux.
8 Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya; kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.
La myrrhe, l'aloès et la casse parfument tous tes vêtements; Dans les palais d'ivoire, le jeu des instruments te réjouit.
9 Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka; ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.
Des filles de rois sont parmi tes dames d'honneur; A ta droite se tient la reine, parée de l'or d'Ophir.
10 Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu; iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.
Écoute, ma fille, vois et prête l'oreille; Oublie ton peuple et la maison de ton père.
11 Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako; mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.
Le roi désire pour lui ta beauté; Puisqu'il est ton seigneur, prosterne-toi devant lui.
12 Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso, amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.
La fille de Tyr, chargée de présents, Ainsi que les plus riches du peuple, Viendront te rendre hommage.
13 Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake, chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.
Elle s'avance rayonnante de gloire, la fille du roi; Son vêtement est tissé d'or.
14 Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu; anamwali okhala naye akumutsatira ndipo abweretsedwa kwa inu.
Elle est présentée au roi, revêtue d'habits brodés. A sa suite, des vierges, ses compagnes, Sont amenées en sa présence.
15 Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo; akulowa mʼnyumba yaufumu.
Elles sont introduites, Au milieu des chants de joie et d'allégresse; Elles entrent dans le palais du roi.
16 Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako; udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.
Tes fils, ô roi, occuperont la place de tes pères; Tu les établiras princes sur toute la terre.
17 Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse; choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.
Je rendrai ton nom célèbre dans tous les âges; Aussi les peuples te loueront-ils éternellement, à perpétuité.

< Masalimo 45 >