< Masalimo 45 >

1 Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati. Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu; lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.
Přednímu kantoru z synů Chóre, na šošannim, vyučující. Píseň o lásce. Vyneslo srdce mé slovo dobré, vypravovati budu písně své o králi, jazyk můj jako péro hbitého písaře.
2 Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika, popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.
Krásnější jsi nad všecky syny lidské, rozlita jest i milost ve rtech tvých, proto že jest tobě požehnal Bůh až na věky.
3 Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu; mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.
Připaš meč svůj na bedra, ó reku udatný, prokaž důstojnost a slávu svou.
4 Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo; dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.
A v té slávě své šťastně vyjížděj s slovem pravdy, tichosti a spravedlnosti, a dokáže pravice tvá hrozných věcí.
5 Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu, mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.
Střely tvé jsou ostré, padati budou od nich před tebou národové, proniknou až k srdci nepřátel královských.
6 Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi; ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.
Trůn tvůj, ó Bože, jest věčný a stálý, berla království tvého jestiť berla nejupřímější.
7 Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.
Miluješ spravedlnost, a nenávidíš bezbožnosti, protož pomazal tě, Bože, Bůh tvůj olejem veselé nad účastníky tvé.
8 Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya; kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.
Mirra, aloe a kassia, všecka roucha tvá voní z paláců, z kostí slonových vzdělaných, nad ty, jenž tě obveselují.
9 Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka; ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.
Dcery králů jsou mezi vzácnými tvými, přístojíť i manželka tobě po pravici v ryzím zlatě.
10 Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu; iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.
Slyšiž, dcerko, a viz, a nakloň ucha svého, a zapomeň na lid svůj a na dům otce svého.
11 Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako; mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.
I zalíbí se králi tvá krása; onť jest zajisté Pán tvůj, protož skláněj se před ním.
12 Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso, amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.
Tuť i Tyrští s dary, před oblíčejem tvým kořiti se budou bohatí národové.
13 Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake, chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.
Všecka slavná jest dcera královská u vnitřku, roucho zlatem vytkávané jest oděv její.
14 Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu; anamwali okhala naye akumutsatira ndipo abweretsedwa kwa inu.
V rouše krumpovaném přivedena bude králi, i panny za ní, družičky její, přivedeny budou k tobě.
15 Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo; akulowa mʼnyumba yaufumu.
Přivedeny budou s radostí velikou a plésáním, a vejdou na palác královský.
16 Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako; udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.
Místo otců svých budeš míti syny své, kteréž postavíš za knížata po vší zemi.
17 Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse; choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.
V pamět uvoditi budu jméno tvé po všecky věky, pročež oslavovati tě budou národové na věky věků.

< Masalimo 45 >